Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 December tsamba 7
  • Chikondi Chenicheni

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chikondi Chenicheni
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Tetezani Banja Lanu
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Mungapeze Nzeru Zokuthandizani pa JW.ORG
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani Yokhala Pabanja Ndi Kusakhala Pabanja?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 December tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Chikondi Chenicheni

Yehova poyambitsa ukwati, anafuna kuti mwamuna ndi mkazi akakwatirana azikhala limodzi kwa moyo wonse. (Gen. 2:22-24) Munthu angasankhe kuthetsa ukwati pokhapokha ngati wina wachita chigololo. (Mal. 2:16; Mat. 19:9) Popeza Yehova amafuna kuti anthu okwatirana azikhala mosangalala, anapereka malangizo othandiza Akhristu kuti azitha kusankha bwino munthu wokwatirana naye n’cholinga choti akhale ndi mabanja abwino.​—Mlal. 5:4-6.

ONERANI VIDIYO YAKUTI CHIKONDI CHENICHENI KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Liz akucheza ndi bambo ake

    N’chifukwa chiyani malangizo omwe Liz analandira kwa bambo ndi mayi ake ali anzeru komanso othandiza?

  • N’chifukwa chiyani si nzeru kuganiza kuti mungathe kusintha khalidwe la munthu amene muli naye pa chibwenzi?

  • Kodi m’bale ndi mlongo Foster anapereka malangizo otani kwa Liz?

  • Zack ndi Magi ali ku Nyumba ya Ufumu

    Kodi mavuto anayamba bwanji m’banja la Zack ndi Magi?

  • Liz ndi John ali ku Nyumba ya Ufumu

    Kodi John ndi Liz anali ndi zolinga zauzimu ziti zomwe zinali zofanana?

  • N’chifukwa chiyani musanakwatirane mumafunika kudziwa “munthu wobisika wamumtima” wa munthu amene mukufuna kukwatirana naye? (1 Pet. 3:4)

  • Kodi chikondi chenicheni tingachidziwe bwanji? (1 Akor. 13:4-8)

Kodi Akhristu angapeze kuti mfundo zina zothandiza pa nkhani zokhudza chibwenzi?

  • Mavidiyo a pa JW Broadcasting akuti Kukonzekera Banja

  • Vidiyo ya pa JW.ORG yakuti Kodi Ndi Chikondi Chenicheni Kapena Kungotengeka Maganizo?

  • Buku loyamba ndi lachiwiri la Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa

  • Buku la Mboni za Yehova Lofufuzira Nkhani (Pitani pamene alemba kuti “Moyo Wabanja,” kenako pamene alemba kuti “Kupeza Chibwenzi.”)

Kodi okwatirana angapeze kuti malangizo othandiza kuti banja lawo liziyenda bwino?

  • Nkhani za pa JW. ORG (Pitani pamene alemba kuti ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA > MALANGIZO OTHANDIZA BANJA LONSE.)

  • Kabuku kakuti Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala

  • Buku lakuti Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja

  • Buku la Mboni za Yehova Lofufuzira Nkhani (Pitani pamene alemba kuti “Moyo Wabanja,” kenako pamene alemba kuti “Banja.”)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena