Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • th phunziro 12 tsamba 15
  • Kulankhula Mwachikondi Komanso Mokoma Mtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulankhula Mwachikondi Komanso Mokoma Mtima
  • Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Nkhani Yofanana
  • Kulankhula ndi Mtima Wonse
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Kuwafika Pamtima Anthu
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Mzimu Waubwenzi ndi Mmene Mukumvera
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kulankhula Mokambirana ndi Anthu
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
Onani Zambiri
Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
th phunziro 12 tsamba 15

PHUNZIRO 12

Kulankhula Mwachikondi Komanso Mokoma Mtima

Lemba

1 Atesalonika 2:7, 8

MFUNDO YAIKULU: Mukamalankhula, anthu aziona kuti mumawaganizira komanso mumawafunira zabwino.

MMENE MUNGACHITIRE:

  • Muziganizira anthu. Pokonzekera nkhani yanu muziganizira mavuto amene anthu akukumana nawo. Muziganiziranso mmene anthuwo akumvera chifukwa cha mavuto awo.

  • Muzisankha bwino mawu. Cholinga chanu chizikhala kuwalimbikitsa, kuwatonthoza komanso kuwapatsa mphamvu. Pewani kukhumudwitsa anthu, kudzudzula anthu omwe si Mboni kapena kutsutsa kwambiri mfundo zimene anthu ena amazikhulupirira kwambiri.

  • Muzisonyeza kuti mumakonda anthu. Mawu komanso nkhope yanu zizisonyeza kuti mumaganizira anthu. Muzikondanso kumwetulira.

    Mfundo yothandiza

    Koma sikuti muzichita zinthu mokakamizika kapena mokokomeza. Ngati mukuwerenga, mawu anu azimveka mogwirizana ndi uthenga umene mukuwerengawo. Muziyesetsa kulankhula mwachikondi komanso mokoma mtima.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena