-
Kukwaniritsa Kudzipatulira KwathuUtumiki wa Ufumu—2003 | January
-
-
Kukwaniritsa Kudzipatulira Kwathu
1 Mwina mwabatizidwa posachedwapa kapena munabatizidwa kale. Mulimonsemo, mukukumbukirabe chochitika chapadera chimenechi pamoyo wanu. Ubatizo wathu sindiwo mapeto a zonse ayi koma ndi kuyamba kwa utumiki wodzipatulira wa moyo wathu wonse umene ungafike mpaka muyaya. (1 Yoh. 2:17) Kodi kukwaniritsa kudzipatulira kwathu kumafunikira chiyani?
2 Kutsanzira Chitsanzo cha Kristu: Yesu atabatizidwa, “anayamba ntchito yake” yolalikira “Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu.” (Luka 3:23; 4:43) Ifenso tikasonyeza kudzipatulira kwathu kwa Yehova mwa ubatizo, timakhala atumiki oikidwa a uthenga wabwino. Ngakhale kuti m’pofunika nthaŵi ndi khama kuti tipeze zofunika pamoyo, ntchito yathu yaikulu ndiyo utumiki wachikristu. (Mat. 6:33) M’malo mofunitsitsa chuma kapena kutchuka, anthu odzipatulira kwa Mulungu amafuna ‘kulemekeza utumiki wawo’ ngati mmene mtumwi Paulo anachitira. (Aroma 11:13) Kodi mumaukonda ndi mtima wonse mwayi wanu wotumikira Yehova ndi kuchita utumikiwo mwakhama?
3 Mofanana ndi mmene Yesu anachitira, tifunika ‘kukaniza Mdyerekezi.’ (Yak. 4:7) Yesu atabatizidwa, Satana anamuyesa, ndipo amateronso ndi atumiki a Yehova odzipatulira masiku ano. (Luka 4:1-13) Popeza kuti tikukhala m’dziko la Satana, tifunika kudziletsa ndi kupeŵa chilichonse chimene chingadetse maganizo athu kapena kuipitsa mtima wathu. (Miy. 4:23; Mat. 5:29, 30) Akristu akulangizidwa kuti ‘sangathe kulandirako ku gome la Ambuye, ndi ku gome la ziwanda.’ (1 Akor. 10:21) Zimenezi zimafuna kuti tipeŵe zinthu zoipa pamene tikusangalala, mayanjano oipa, ndi zoipa zimene tingakumane nazo pogwiritsira ntchito makompyuta. Zimafunanso kuti tipeŵe zinthu zokhudzana ndi ampatuko. Kukhala maso pa machenjera ameneŵa ndi enanso a Satana kudzatithandiza kukwaniritsa kudzipatulira kwathu.
4 Kugwiritsira Ntchito Zimene Mulungu Watipatsa: Pofuna kutithandiza kukwaniritsa kudzipatulira kwathu, Yehova wapereka thandizo la Mawu ake ndi mpingo wachikristu. Khalani ndi chizoloŵezi choŵerenga Baibulo ndi kupemphera kwa Yehova tsiku ndi tsiku. (Yos. 1:8; 1 Ates. 5:17) Sangalalani ndi misonkhano ya mpingo. (Sal. 122:1) Yanjanani ndi anthu oopa Yehova amene amasunga malamulo ake.—Sal. 119:63.
5 Pothandizidwa ndi Yehova, mutha kukwaniritsa kudzipatulira kwanu kwa iye ndi kukhala ndi mwayi wom’tumikira mpaka muyaya.—Sal. 22:26, 27; Afil. 4:13.
-
-
Ntchito Imene Imafunika KudzichepetsaUtumiki wa Ufumu—2003 | January
-
-
Ntchito Imene Imafunika Kudzichepetsa
1 Mawu a Mulungu amatilangiza kuti tikhale “odzichepetsa; osabwezera choipa ndi choipa, . . . koma . . . [kupereka, NW] madalitso.” (1 Pet. 3:8, 9) Mosakayikira, uphungu umenewu umagwira ntchito polalikira. Inde, utumiki wachikristu ungatiyese pa kudzichepetsa kwathu.
2 Khalidwe la kudzichepetsa limatithandiza kupirira zovuta zimene tingakumane nazo. Tikamalalikira, timapita tokha asanatiitane ndi kukalankhula ndi anthu osawadziŵa, ndipo timadziŵa kuti ena satilandira bwino. Kuti tilalikirebe tikakumana ndi anthu osatilandira bwinoŵa, m’pofunika kudzichepetsa. M’gawo lina louma kwambiri, alongo aŵiri omwe ndi apainiya anayenda khomo ndi khomo tsiku lililonse kwa zaka ziŵiri popanda kulankhula ndi munthu wina aliyense! Koma analimbikira, ndipo lero kumeneko kuli mipingo iŵiri.
3 Ngati Tichitiridwa Chipongwe: Ena akapanda kutikomera mtima kapena akatichitira chipongwe, kudzichepetsa kudzatithandiza kutsanzira Yesu. (1 Pet. 2:21-23) Panyumba ina, mlongo wina anatukwanidwa, koyamba ndi mkazi kenako ndi mwamuna wa mkaziyo amene anam’thamangitsa. Asanachoke, mlongoyo anangomwetulira ndipo anati adzalankhula nawo nthaŵi ina. Zimenezi zinadabwitsa kwambiri banjalo moti pamene wa Mboni wina anafika, iwo anamvetsera. Atawapempha kupita ku msonkhano ku Nyumba ya Ufumu, iwo anavomera. Mlongo anam’thamangitsa uja anali komweko ndipo anawapatsa moni ndi kuwalalikiranso. Ifenso tingafeŵetse mitima ya anthu osafuna kumva mwa kusonyeza “chifatso ndi mantha.”—1 Pet. 3:15; Miy. 25:15.
4 Peŵani Kudzitukumula: Kudziŵa kwathu Baibulo sikutipatsa chifukwa choti tiziderera anthu ena kapena kuwanyoza. (Yoh. 7:49) M’malo mwake, Mawu a Mulungu amatilangiza ‘kusachitira mwano munthu aliyense.’ (Tito 3:2) Tikakhala a mtima wodzichepetsa ngati mmene Yesu analili, timapumulitsa ena. (Mat. 11:28, 29) Kukhala odzichepetsa kumathandiza kuti uthenga wathu ukhale wokopa anthu.
5 Inde, kudzichepetsa kumatithandiza kupirira m’gawo louma. Kungafeŵetse mitima ya anthu osafuna kumva, ndipo ena amakopeka nako n’kulandira uthenga wa Ufumu. Koposa zonse, kumasangalatsa Yehova, amene “apatsa chisomo kwa odzichepetsa.”—1 Pet. 5:5.
-