Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ntchito Imene Imatsitsimula
    Utumiki wa Ufumu—2003 | August
    • Ntchito Imene Imatsitsimula

      1 Uthenga wa m’Baibulo umatsitsimula anthu onse amene amaulandira ndi kuugwiritsa ntchito pa moyo wawo. (Sal. 19:7, 8) Umawathandiza kumasuka ku ziphunzitso zonyenga ndi kusiya makhalidwe oika moyo pachiswe ndiponso umawapatsa chiyembekezo chodalirika cha m’tsogolo. Komabe, amene amapindula si anthu amene amalandira uthenga wabwino okhawo ayi. Anthu amene amauza ena choonadi chotsitsimula cha m’Baibulo nawonso amatsitsimulidwa.—Miy. 11:25.

      2 Kupeza Mphamvu Chifukwa cha Utumiki: Yesu ananena kuti amene amasenza goli lokhala wophunzira wa Kristu, limene limaphatikizapo ntchito yolalikira ndi kupanga ophunzira, ‘adzapeza mpumulo wa miyoyo yawo.’ (Mat. 11:29) Iyenso payekha anaona kuti kulalikira kwa ena kunam’patsa mphamvu. Kwa iye, ntchito imeneyi inali ngati chakudya. (Yoh. 4:34) Pamene Yesu anatumiza ophunzira 70 kuti akalalikire, ophunzirawo anasangalala ataona kuti Yehova wadalitsa khama lawo.—Luka 10:17.

      3 Mofananamo, Akristu ambiri masiku ano amapezanso mphamvu akamagwira nawo ntchito yolalikira. Mlongo wina anati: “Utumiki ndi wotsitsimula chifukwa umandithandiza kukhala ndi cholinga pa moyo. Mavuto anga ndi nkhaŵa za tsiku ndi tsiku zimachepa ndikamalalikira.” Mtumiki wina wachangu anati: “Utumiki . . . umandichititsa kuti ndizimuona Yehova kukhala weniweni tsiku ndi tsiku ndipo umandithandiza kukhala ndi mtendere komanso chimwemwe cha mumtima chimene sichingapezeke m’njira ina iliyonse.” Tili ndi mwayi waukulu wokhala “antchito anzake a Mulungu.”—1 Akor. 3:9.

      4 Goli la Kristu N’lofeŵa: Ngakhale kuti Akristu akulimbikitsidwa ‘kuyesetsa [“mwakhama,” NW],’ Yesu sakufuna kuti tichite zinthu zimene sitingathe. (Luka 13:24) Ndipotu, amatipempha mwachikondi ‘kusenza goli lake.’ (Mat. 11:29) Amene akukumana ndi mavuto pamoyo wawo angakhulupirire kuti utumiki wawo umene amachita ndi mtima wonse, ngakhale kuti ndi wochepa, umasangalatsa Mulungu.—Marko 14:6-8; Akol. 3:23.

      5 N’zotsitsimula kwambiri kutumikira Mulungu amene amayamikira zilizonse zimene timachita chifukwa cha dzina lake. (Aheb. 6:10) Tiyenitu tiyesetse kum’patsa zonse zimene tingathe.

  • Tsanzirani Ubwino wa Yehova
    Utumiki wa Ufumu—2003 | August
    • Tsanzirani Ubwino wa Yehova

      1 Tikaona kuloŵa kwa dzuŵa kochititsa chidwi kapena tikadya chakudya chokoma kwambiri, kodi sizitichititsa kuyamikira Yehova, yemwe ndi Gwero la zinthu zonse zabwino? Ubwino wake umatichititsa kufuna kumutsanzira. (Sal. 119:66, 68; Aef. 5:1) Kodi tingasonyeze bwanji ubwino?

      2 kwa Anthu Osakhulupirira: Imodzi mwa njira zimene tingatsanzirire ubwino wa Yehova ndiyo mwa kusonyeza ndi mtima wonse kuti timaganizira anthu osakhulupirira. (Agal. 6:10) Kusonyeza ubwino powathandiza kungawachititse kuziona bwino Mboni za Yehova ndiponso uthenga umene timalalikira.

      3 Mwachitsanzo, mpainiya wina wachinyamata ali pa mzera kuti alandire mankhwala pa chipatala china, anakhala pafupi ndi mzimayi wachikulire amene ankaoneka kuti akudwala kwambiri kuposa ambiri mwa anthu amene analipo. Itafika nthaŵi yoti mbaleyo aonane ndi dokotala, anauza mzimayiyo kuti apite m’malo mwa iye. Patapita nthaŵi anadzakumananso, koma panthaŵiyi kunali ku msika ndipo mzimayiyo anasangalala kumuona mbaleyo. Ngakhale kuti poyamba sanali kumvetsera uthenga wabwino, tsopano anati anadziŵa kuti Mboni za Yehova zimakondadi anzawo. Anayamba phunziro la Baibulo la nthaŵi zonse.

      4 kwa Abale Athu: Timatsanziranso ubwino wa Yehova tikamathandiza okhulupirira anzathu. Pakachitika mavuto adzidzidzi, timakhala m’gulu la anthu oyambirira kuthandiza abale athu. Timasonyezanso mtima umenewu pothandiza anthu amene amafuna zoyendera kuti apite ku misonkhano, pochezera anthu odwala chifukwa cha ukalamba, ndiponso posonyeza chikondi kwa anthu amene sitikuwadziŵa bwino mumpingomo.—2 Akor. 6:11-13; Aheb. 13:16.

      5 Njira ina imene Yehova amasonyezera ubwino ndiyo mwa kukhala “wokhululukira.” (Sal. 86:5) Pomutsanzira, tingasonyeze kuti timakonda ubwino mwa kukhululukira ena. (Aef. 4:32) Zimenezi zimathandiza kuti kukhala kwathu pamodzi ndi okhulupirira anzathu kukhale ‘kokoma ndi kokondweretsa.’—Sal. 133:1-3.

      6 Ubwino wochuluka wa Yehova utichititse kum’tamanda kwambiri komanso kukhala ndi chimwemwe chodzaza tsaya. Ndiponso utilimbikitse kuyesetsa kutsanzira ubwino wake pa zonse zimene timachita.—Sal. 145:7; Yer. 31:12.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena