-
Kumbukirani Mkazi wa LotiZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 10
Kumbukirani Mkazi wa Loti
Loti ankakhala ndi Abulahamu ku Kanani. Lotiyu anali mwana wa mng’ono wake wa Abulahamu. Kenako onse anakhala ndi ziweto zambiri moti malo odyetsera ziwetozo anawachepera. Ndiyeno Abulahamu anauza Loti kuti: ‘N’zosatheka kuti tizikhalabe limodzi. Yamba iweyo kusankha kumene ukufuna kukakhala ndipo ine ndipita kwinako.’ Apatu Abulahamu anasonyeza kuti sanali wodzikonda.
Loti anaona dera lapafupi ndi mzinda wa Sodomu limene linali lokongola. Iye anakopeka ndi derali chifukwa linali ndi madzi ambiri komanso udzu wobiriwira. Choncho anasankha dera limeneli ndipo anasamukira kumeneku ndi banja lake.
Anthu a mumzinda wa Sodomu komanso mzinda wina wapafupi wotchedwa Gomora anali ndi makhalidwe oipa kwambiri. Choncho Yehova anaona kuti ndi bwino kungowononga mizindayo. Koma Mulungu anaganiza zoti apulumutse Loti ndi banja lake. Iye anatumiza angelo awiri kukawauza kuti: “Fulumirani! Tulukani mumzinda uno, chifukwa Yehova auwononga.”
Koma Loti ndi banja lake ankangochedwachedwa moti angelowo anachita kuwagwira manja n’kuwatulutsa mumzindawo. Iwo anawauza kuti: ‘Thawani mupulumutse moyo wanu! Musayangʼane kumbuyo chifukwa mukangoyang’ana mufa.’
Iwo atafika mumzinda wa Zowari, Yehova anagwetsa moto ndi sulufule ngati mvula mumzinda wa Sodomu ndi Gomora. Mizinda yonseyi inapseratu. Koma mkazi wa Loti sanamvere Yehova ndipo anayang’ana m’mbuyo. Atangotero anasanduka chipilala chamchere. Komabe Loti ndi ana ake aakazi anapulumuka chifukwa choti anamvera Yehova. Onse ayenera kuti anamva chisoni ataona kuti mayi afa chifukwa chosamvera. Koma anasangalala kuti iwowo anamvera malangizo a Yehova.
“Kumbukirani mkazi wa Loti.”—Luka 17:32
-
-
Abulahamu Anasonyeza Kuti Anali WokhulupirikaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 11
Abulahamu Anasonyeza Kuti Anali Wokhulupirika
Abulahamu anaphunzitsa mwana wake Isaki kuti azikonda Yehova komanso kukhulupirira malonjezo ake onse. Koma Isaki ali ndi zaka pafupifupi 25, Yehova anapempha Abulahamu kuti achite zinthu zovuta kwambiri. Kodi anamuuza kuti achite chiyani?
Mulungu anauza Abulahamu kuti: ‘Tenga mwana wako mmodzi yekhayo ndipo ukamupereke nsembe kuphiri la Moriya.’ Abulahamu sankadziwa chifukwa chake Yehova anamuuza kuti achite zimenezi, komabe iye anamvera.
M’mawa wa tsiku lotsatira, anatenga Isaki komanso antchito ake awiri n’kuyamba ulendo wopita kuphiri la Moriya. Atayenda kwa masiku atatu, anayamba kuona phirilo chapatali. Abulahamu anauza antchito ake aja kuti adikire penapake, pamene iye ndi Isaki akukapereka nsembe. Abulahamu anapatsa Isaki nkhuni kuti anyamule ndipo iye anatenga mpeni. Koma Isaki anafunsa bambo akewo kuti: ‘Nanga nkhosa yokapereka nsembeyo ili kuti?’ Abulahamu anayankha kuti: ‘Mwana wanga, Yehova apereka nkhosa yoti tipereke nsembe.’
Atafika paphiripo, anamanga guwa loti aperekerepo nsembe. Ndiyeno Abulahamu anamanga Isaki manja ndi miyendo n’kumugoneka paguwapo.
Kenako anatenga mpeni kuti amuphe. Koma nthawi yomweyo, anamva mngelo wa Yehova akufuula kuti: ‘Abulahamu, usamuvulaze mwanayo. Tsopano ndadziwa kuti umakhulupirira Mulungu chifukwa umafuna kupereka nsembe mwana wako.’ Zitatero, Abulahamu anaona nkhosa itakodwa m’ziyangoyango, chapafupi. Mwamsanga anamasula Isaki ndipo anatenga nkhosayo n’kuipereka nsembe.
Kuyambira tsiku limenelo, Yehova anayamba kutchula Abulahamu kuti mnzake. Kodi ukudziwa chifukwa chake? Ndi chifukwa choti Abulahamu ankachita zilizonse zimene Yehova ankafuna ngakhale zitakhala kuti sakuzimvetsa.
Yehova anabwerezanso lonjezo limene anamuuza Abulahamu kuti: ‘Ndidzakudalitsa komanso ndidzachulukitsa ana ako kapena kuti mbadwa zako.’ Apa Yehova ankatanthauza kuti adzadalitsa anthu onse abwino kudzera m’banja la Abulahamu.
“Mulungu anakonda kwambiri dziko moti anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense womukhulupirira asawonongedwe koma akhale ndi moyo wosatha.”—Yohane 3:16
-