Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Yobu Anali Ndani?
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Yobu ali ndi zilonda thupi lonse ndipo anthu atatu apita kukamuona

      MUTU 16

      Kodi Yobu Anali Ndani?

      Kudziko lina lotchedwa Uzi kunali munthu wina amene ankalambira Yehova. Dzina lake anali Yobu. Iye anali ndi banja lalikulu ndipo anali wolemera kwambiri. Yobu anali wokoma mtima ndipo ankathandiza anthu osauka, azimayi amasiye komanso ana amasiye. Koma kodi iye sakanakumana ndi mavuto chifukwa choti anali munthu wabwino? Ayi.

      Satana Mdyerekezi

      Satana Mdyerekezi ankaona zonse zimene Yobu ankachita, ngakhale kuti Yobuyo sankadziwa zimenezi. Yehova anauza Satana kuti: ‘Kodi waona mtumiki wanga Yobu? Padziko lapansi palibe munthu wolungama ngati iyeyu. Iye amandimvera komanso amachita zoyenera.’ Satana anayankha kuti: ‘N’zoona kuti Yobu amakumverani. Koma n’chifukwa choti mumamuteteza komanso kumudalitsa. Mwamupatsa malo abwino komanso ziweto. Koma mutamulanda zinthu zimenezi akhoza kusiya kukulambirani.’ Yehova anati: ‘Ndakulola kuti umuyese, koma usamuphe.’ N’chifukwa chiyani Yehova analola kuti Satana ayese Yobu? N’chifukwa choti ankadziwa kuti Yobu akhalabe wokhulupirika.

      Satana anayamba kuyesa Yobu pomubweretsera mavuto osiyanasiyana. Choyamba anachititsa kuti anthu otchedwa Asabeya abe ng’ombe ndi abulu a Yobu. Kenako moto unatentha nkhosa zake. Ndiye panabweranso anthu otchedwa Akasidi amene anadzaba ngamila zake zonse. Komanso antchito amene ankayang’anira ziweto za Yobu anaphedwa. Komatu si zokhazi. Tsiku lina ana onse a Yobu anali m’nyumba ina n’kumachita phwando. Koma mwadzidzidzi nyumbayo inagwa n’kupha onsewo. Yobu anamva chisoni kwambiri ndi zonsezi komabe sanasiye kulambira Yehova.

      Satana anaganiza kuti Yobu akhoza kusiya kumvera Mulungu atakumana ndi mavuto enanso. Choncho anachititsa kuti Yobu atuluke zilonda zowawa kwambiri thupi lonse. Yobu anali pa ululu woopsa. Iye sankadziwa chimene chinkachititsa zonsezi koma anapitiriza kulambira Yehova. Mulungu ankaona zonsezi ndipo anasangalala kwambiri kuona kuti Yobu anakhalabe wokhulupirika.

      Kenako Satana anatumiza azibambo atatu kuti akayese Yobu. Iwo anauza Yobu kuti: ‘Uyenera kuti unachimwira Mulungu ndipo unabisa. Ndiye Mulungu akukulanga chifukwa cha zimenezo.’ Yobu anati: ‘Palibe chilichonse cholakwika chimene ndinachita.’ Koma zitatere Yobu anayamba kuganiza kuti Yehova ndi amene akuchititsa mavuto ake ndipo sakuchita chilungamo.

      Munthu wina wamng’ono kuposa azibambo atatu aja, dzina lake Elihu, ankangomvetsera pamene anthuwa ankakambirana. Koma kenako anayankha kuti: ‘Zimene nonsenu mukunena si zoona. Yehova ndi wapamwamba kwambiri ndipo anthufe sitingathe kumvetsa zochita zake zonse. Iye sangachite zinthu zoipa. Amaona zonse ndipo anthu akamavutika amawathandiza.’

      Yobu ndi mkazi wake ali ndi mwana

      Ndiyeno Yehova analankhula ndi Yobu kuti: ‘Kodi unali kuti pamene ndinkalenga kumwamba ndi dziko lapansi? N’chifukwa chiyani ukunena kuti ndikuchita zinthu zopanda chilungamo? Ukungolankhulatu zinthu zimene sukuzidziwa.’ Yobu anazindikira kuti ankaganiza molakwika ndipo anati: ‘Pepani ndalakwa. Ndinkangomva za inu, koma panopa ndakudziwani. Palibe chimene simungathe kuchita. Mundikhululukire chifukwa cha zomwe ndinanena.’

      Kenako mayesero a Yobu anatha ndipo Yehova anamuchiritsa. Anamupatsanso zinthu zambiri kuposa zomwe anali nazo poyamba. Yobu anakhala ndi moyo wosangalala komanso wautali. Yehova anamudalitsa chifukwa choti ankamumvera ngakhale pa mavuto. Kodi iwenso ungakhale ngati Yobu n’kumalambira Yehova zivute zitani?

      “Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mukudziwa madalitso amene Yehova anamupatsa.”​—Yakobo 5:11

      Mafunso: Kodi Satana anachititsa kuti Yobu akumane ndi mayesero ati? Kodi Yehova anadalitsa bwanji Yobu?

      Yobu 1:1–3:26; 4:7; 32:1-5; 34:5, 21; 35:2; 36:15, 26; 38:1-7; 40:8; 42:1-17

  • Mose Anasankha Kuti Azilambira Yehova
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Mwana wa Farao wapeza Mose ndipo Miriamu waima chapafupi

      MUTU 17

      Mose Anasankha Kuti Azilambira Yehova

      Ku Iguputo, anthu a m’banja la Yakobo anayamba kudziwika kuti Aisiraeli. Yakobo ndi Yosefe atamwalira, Farao wina anayamba kulamulira. Iye ankachita mantha chifukwa Aisiraeli anali amphamvu kuposa Aiguputo. Choncho Farao ameneyu anachititsa kuti Aisiraeli akhale akapolo. Anawalamula kuti aziumba njerwa komanso kugwira ntchito zotopetsa kumunda. Koma ngakhale kuti ankazunzidwa kwambiri ndi Aiguputo, Aisiraeli anapitirizabe kuchulukana. Popeza Farao sankafuna zimenezi, analamula kuti ana onse aamuna a Aisiraeli aziphedwa akangobadwa. Ukuganiza kuti Aisiraeli anamva bwanji lamuloli litaperekedwa?

      Izi zitachitika, mayi wina wa Chiisiraeli, dzina lake Yokebedi anabereka mwana wamwamuna wokongola kwambiri. Pofuna kuteteza mwanayo, mayiyo anamuika m’basiketi n’kukamubisa m’mabango, mumtsinje wa Nailo. Mchemwali wake wa mwanayo, dzina lake Miriamu, anakhala chapafupi kuti azimuyang’anira.

      Ndiyeno mwana wamkazi wa Farao anabwera kuti adzasambe ndipo anaona basiketi ija. Atatsegula basiketiyo anapeza kuti munali mwana. Mwanayo ankalira ndipo anamumvera chisoni. Miriamu anafunsa mwana wamkazi wa Faraoyo kuti: ‘Kodi mungakonde kuti ndikakufufuzireni mzimayi woti azimusamalira?’ Mwana wa Farao atavomera, Miriamu anapita n’kukauza amayi ake, a Yokebedi. Atabwera, mwana wa Faraoyo anawauza kuti: ‘Tengani mwanayu, muzikamusamalira ndipo ndizikulipirani.’

      Mose akuthawa

      Mwana uja atakula, Yokebedi anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anamupatsa dzina loti Mose n’kumakhala naye ngati mwana wake. Mose analeredwa ngati mwana wa mfumu ndipo akanatha kupeza chilichonse chimene ankafuna. Koma iye sanaiwale Yehova. Ankadziwa kuti anali wa ku Isiraeli osati wa ku Iguputo ndipo anasankha kuti azitumikira Yehova.

      Ali ndi zaka 40, Mose ankafuna kuthandiza Aisiraeli anzake. Choncho ataona munthu wa ku Iguputo akumenya munthu wa Chiisiraeli, Mose anamenya munthu wa ku Iguputoyo mpaka kumupha. Atatero anakwirira munthu wakufayo mumchenga. Farao atadziwa zimenezi, ankafuna kupha Mose. Choncho Mose anathawira ku Midiyani. Kumeneko, Yehova anali naye.

      “Chifukwa cha chikhulupiriro, Mose . . . anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao, ndipo anasankha kuzunzidwa limodzi ndi anthu a Mulungu.”​—Aheberi 11:24, 25

      Mafunso: Kodi Aisiraeli anakumana ndi zotani ku Iguputo? Kodi n’chifukwa chiyani Mose anathawira ku Midiyani?

      Genesis 49:33; Ekisodo 1:1-14, 22; 2:1-15; Machitidwe 7:17-29; Aheberi 11:23-27

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena