-
Anaona Chitsamba ChikuyakaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 18
Anaona Chitsamba Chikuyaka
Mose anakhala ku Midiyani kwa zaka 40. Iye anakwatira n’kukhala ndi ana. Tsiku lina akudyetsa nkhosa pafupi ndi phiri la Sinai, anaona zinthu zodabwitsa. Anaona chitsamba chikuyaka koma sichinkapsa. Atayandikira kuti aone zimene zikuchitika, anamva mawu ochokera m’chitsambacho akuti: ‘Mose! Usayandikire kuno. Vula nsapato zakozo chifukwa malo amene waimawo ndi oyera.’ Yehova ndi amene ankamulankhula ndipo anagwiritsa ntchito mngelo.
Mose anachita mantha kwambiri moti anaphimba nkhope yake. Yehova anamuuza kuti: ‘Ndaona kuti Aisiraeli akuvutika kwambiri. Ndikufuna kuwapulumutsa ku Iguputo n’kuwapititsa kudziko labwino. Iweyo ndi amene uwatsogolere pochoka ku Iguputo.’ Mose ayenera kuti anadabwa kwambiri ndi zimenezi.
Iye anafunsa kuti: ‘Nanga akakandifunsa kuti wakutuma ndi ndani, ndikayankhe kuti chiyani?’ Mulungu anamuuza kuti: ‘Ukawauze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakobo, ndi amene wandituma kwa inu.’ Kenako Mose anati: ‘Nanga akakapanda kundimvera?’ Yehova anapatsa Mose umboni womutsimikizira kuti adzamuthandiza. Yehova anamuuza kuti aponye ndodo yake pansi. Nthawi yomweyo ndodoyo inasanduka njoka. Koma ataigwira kumchira, inasandukanso ndodo. Ndiyeno Yehova anamuuza kuti: ‘Ukakachita zimenezi, akakhulupirira kuti ndakutumadi.’
Koma Mose anati: ‘Pajatu ine ndimavutika kulankhula.’ Ndiyeno Yehova anamulonjeza kuti: ‘Ineyo ndizikakuuza zoyenera kunena ndipo ndikupatsa m’bale wako Aroni kuti azikakuthandiza.’ Mose atadziwa kuti Yehova amuthandiza, anatenga mkazi ndi ana ake n’kuyamba ulendo wopita ku Iguputo.
“Musadzade nkhawa kuti mudzalankhula bwanji kapena kuti mudzanena chiyani, chifukwa zoti mulankhule mudzapatsidwa nthawi yomweyo.”—Mateyu 10:19
-
-
Miliri Itatu YoyambiriraZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 19
Miliri Itatu Yoyambirira
Aiguputo ankaumiriza Aisiraeli kuti azigwira ntchito ngati akapolo. Yehova anatumiza Mose ndi Aroni kwa Farao kukanena kuti: ‘Yehova akuti mulole kuti anthu ake apite kuchipululu kuti akamulambire.’ Koma Farao anayankha mwamwano kuti: ‘Zimene Yehova wanenazo ndilibe nazo ntchito. Sindilola kuti Aisiraeli apite.’ Atatero anawonjezera ntchito zimene Aisiraeli ankagwira. Choncho Yehova anafuna kuti Farao adziwe kuti iye ndi wamkulu kuposa milungu yonse. Kodi ukudziwa zimene anachita? Anabweretsa Miliri 10 ku Iguputo. Yehova anauza Mose kuti: ‘Farao sakufuna kundimvera. Mawa m’mawa akhala ali kumtsinje wa Nailo. Upite ukamuuze kuti popeza sakufuna kuti anthu anga apite, madzi onse a mumtsinje wa Nailo asanduka magazi.’ Mose anamvera Yehova ndipo anapitadi kwa Farao. Kumeneko Aroni anamenya ndi ndodo madzi a mumtsinje wa Nailo, Farao akuona ndipo madziwo anasanduka magazi. Madziwo anayamba kununkha, nsomba zonse zinafa ndipo anthu anasowa madzi akumwa. Koma Farao sanalolebe kuti Aisiraeli apite.
Patatha masiku 7, Yehova anatumanso Mose kwa Farao kukamuuza kuti: ‘Ukapanda kulola kuti anthu anga apite, m’dziko la Iguputo mudzakhala achule paliponse.’ Aroni anakweza ndodo yake m’mwamba ndipo achule anayamba kudzaza m’dziko lonse. Achulewo ankapezeka m’nyumba, pabedi, m’mbale, tingoti paliponse. Zitatero Farao anauza Mose kuti akapemphe kwa Yehova kuti mliriwu uthe ndipo analonjeza kuti alola Aisiraeli kuti apite. Choncho Yehova anathetsadi mliriwo ndipo achulewo anayamba kufa. Aiguputo anaunjika achulewo milumilu moti dziko lonse linkanunkha. Koma Farao ataona kuti mliri watha, sanalolebe kuti Aisiraeli apite.
Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: ‘Aroni amenye pansi ndi ndodo ndipo fumbi lisanduka tizilombo toyamwa magazi.’ Aroni anachitadi zimenezi ndipo paliponse panagwa tizilombo toyamwa magazi. Aiguputo ena anauza Farao kuti: ‘Mliriwu wachokera kwa Mulungu.’ Koma Farao sanalolebe kuti Aisiraeli apite.
“Ndiwachititsa kuti adziwe mphamvu ndi nyonga zanga, ndipo adziwa kuti dzina langa ndine Yehova.”—Yeremiya 16:21
-