Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w20 September tsamba 31
  • Mafunso Ochokera Kwa Owerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera Kwa Owerenga
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Boma
    Kukambitsirana za m’Malemba
  • Lingaliro Lachikristu la Ulamuliro
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Boma la Mulungu la Mtendere
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2020
w20 September tsamba 31
Chithunzi chosonyeza Yehova atakhala pampando wachifumu wonyezimira ndipo wazunguliridwa ndi angelo ambirimbiri. Malo onse ozungulira mpando wachifumuwo akuwala kwambiri.

Mafunso Ochokera Kwa Owerenga

Kodi lemba la Mlaliki 5:8 limanena za olamulira a anthu, kapena za Yehova?

Lembali ndi lochititsa chidwi chifukwa limati: “Ukaona munthu wosauka akuponderezedwa ndiponso zinthu zachiwawa ndi zopanda chilungamo zikuchitika m’chigawo cha dziko, usadabwe nazo. Pakuti wamkulu kuposa amene akuchita zimenezoyo akuona, ndipo pamwamba pa akuluakuluwo palinso ena akuluakulu kuposa iwowo.”​—Mlal. 5:8.

Popanda kuganizira mmene Yehova amaonera zinthu, tingaone ngati vesili likungonena zimene olamulira maboma a anthu amachita. Koma tikaliganizira kwambiri, tingaone kuti likunenanso za Yehova, zomwe zingatitonthoze ndi kutilimbikitsa.

Lemba la Mlaliki 5:8 limanena za olamulira amene amapondereza osauka komanso kuwachitira zopanda chilungamo. Wolamulira ayenera kukumbukira kuti pali munthu winanso amene amamuyang’anira, yemwe ndi waudindo waukulu kuposa iyeyo. Ndiponso pamwamba pa munthu waudindo waukuluyu, pangakhale enanso a maudindo aakulu kwambiri. Chomvetsa chisoni n’chakuti m’maboma a anthu, olamulira onsewa amakhala achinyengo ndipo anthu amavutika ndi katangale komanso zinthu zopanda chilungamo.

Ngakhale zili choncho, sitiyenera kutaya mtima chifukwa tikudziwa kuti Yehova, amaona zimene anthu a maudindo aakulu m’maboma a anthu amachita. Choncho tingapemphe Yehova kuti atithandize komanso tingathe kumutulira nkhawa zathu. (Sal. 55:22; Afil. 4:6, 7) Timadziwa kuti “maso a Yehova akuyendayenda padziko lonse lapansi kuti aonetse mphamvu zake kwa anthu amene mtima wawo uli wathunthu kwa iye.”​—2 Mbiri 16:9.

Choncho lemba la Mlaliki 5:8 limatikumbutsa zomwe zimachitikadi m’maboma a anthu, kuti nthawi zonse munthu waudindo waukulu, amakhalanso ndi wina waudindo waukulu kuposa iyeyo. Chofunika kwambiri n’chakuti vesili lingatithandize kuganizira mfundo yakuti Yehova ndi amene ali wamkulu kwambiri, iye ndi Wolamulira Wamkulu. Panopa Yehova akulamulira kudzera mwa Mwana wake Yesu Khristu, yemwe ndi Mfumu ya Ufumu wa Mulungu. Yehova yemwe ndi Wamphamvuyonse amaona zinthu zonse komanso munthu aliyense ndipo iye komanso Mwana wake ndi achilungamo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena