Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Gidiyoni Anagonjetsa Amidiyani
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Gidiyoni ndi asilikali ake aliza malipenga, kuphwanya mitsuko, kunyamula zounikira m’mwamba kenako n’kufuula

      MUTU 34

      Gidiyoni Anagonjetsa Amidiyani

      Patapita nthawi, Aisiraeli anasiyanso kulambira Yehova ndipo anayamba kulambira milungu yabodza. Kwa zaka 7, Amidiyani ankaba ziweto za Aisiraeli komanso kuwawonongera mbewu zawo. Pothawa Amidiyaniwo, Aisiraeli ankabisala m’mapanga komanso m’mapiri. Kenako anapempha Yehova kuti awapulumutse. Ndiyeno Yehova anatumiza mngelo kuti apite kwa Gidiyoni. Mngeloyo anauza Gidiyoni kuti: ‘Yehova wakusankha kuti ukhale msilikali wamphamvu.’ Gidiyoni anafunsa kuti: ‘Kodi munthu wachabechabe ngati ine, ndingapulumutse bwanji Aisiraeli?’

      Koma kodi Gidiyoni akanatsimikizira bwanji kuti Yehova anamusankhadi? Iye anaika pansi ubweya wa nkhosa n’kuuza Yehova kuti: ‘Ngati m’mawa, ubweyawu unganyowe ndi mame koma nthaka n’kukhala youma, ndidzadziwa kuti mwandisankhadi kuti ndipulumutse Aisiraeli.’ M’mawa wa tsiku lotsatira anapeza kuti ubweya uja wanyowa koma nthaka ndi youma. Koma Gidiyoni anapemphanso kuti m’mawa wa tsiku lotsatira apeze ubweya uja uli wouma koma nthaka idzakhale yonyowa. Zimenezi zitachitika, Gidiyoni anatsimikizira kuti Yehova anamusankhadi. Ndiyeno anasonkhanitsa asilikali ake kuti akamenyane ndi Amidiyani.

      Yehova anauza Gidiyoni kuti: ‘Ndithandiza Aisiraeli kuti apambane pa nkhondoyi. Koma chifukwa uli ndi asilikali ambiri, ungaganize kuti mwapambana ndi mphamvu zanu. Uza aliyense amene akuchita mantha kuti abwerere.’ Choncho asilikali 22,000 anabwerera n’kutsala okwana 10,000. Yehova ananena kuti: ‘Asilikaliwa achulukabe. Pita nawo kumtsinje ndipo ukawauze kuti akamwe madzi. Ndiyeno ukasankhe omwe azikamwa madzi, uku akuyang’ana adani awo.’ Asilikali 300 okha ndi amene anali tcheru pamene ankamwa. Yehova analonjeza kuti asilikali ochepawo adzagonjetsa asilikali a Amidiyani okwana 135,000.

      Usiku, Yehova anauza Gidiyoni kuti: ‘Tsopano pitani mukamenyane ndi Amidiyani. Gidiyoni anapatsa asilikali akewo malipenga a nyanga ndi mitsuko ikuluikulu ndipo m’mitsukomo anaikamo zounikira. Iye anawauza kuti: ‘Muzionetsetsa zimene ndikuchita ndipo nanunso muzichita zomwezo.’ Gidiyoni analiza lipenga lake, n’kuphwanya mtsuko uja ndiyeno ananyamula chounikira chake m’mwamba n’kufuula kuti: ‘Nkhondo ya Yehova ndi ya Gidiyoni!’ Asilikali 300 aja anachitanso chimodzimodzi. Amidiyani atamva zimenezi anachita mantha ndipo anayamba kuthawa. Chifukwa chosokonezeka, iwo anayamba kuukirana okhaokha. Apa Yehova anathandiza Aisiraeli kugonjetsa adani awo.

      Asilikali achimidiyani akuchita mantha

      “Kuti mphamvu yoposa yachibadwa ichokere kwa Mulungu, osati kwa ife.”​—2 Akorinto 4:7

      Mafunso: Kodi Yehova anamutsimikizira bwanji Gidiyoni kuti wamusankha kuti akagonjetse Amidiyani? N’chifukwa chiyani Gidiyoni anali ndi asilikali 300 okha?

      Oweruza 6:1-16; 6:36-40; 7:25; 8:28

  • Hana Anapempha Kuti Mulungu Amupatse Mwana Wamwamuna
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Hana akupereka Samueli kwa Eli kuti azitumikira pachihema

      MUTU 35

      Hana Anapempha Mwana Wamwamuna

      Bambo wina wa ku Isiraeli dzina lake Elikana anali ndi akazi awiri. Mayina a akaziwo anali Hana ndi Penina. Koma Elikana ankakonda kwambiri Hana. Penina anali ndi ana ambiri koma Hana analibe ngakhale mmodzi. Chifukwa cha zimenezi, Penina ankanyoza Hana nthawi zonse. Chaka chilichonse, Elikana ankapita kukalambira Mulungu ku Silo limodzi ndi banja lake. Tsiku lina ali kumeneko, anazindikira kuti mkazi wake Hana, amene ankamukonda kambiri, wakhumudwa kwambiri. Iye anamuuza kuti: ‘Hana usalire. Ndimakukonda kwambiri. Kodi si ine woposa ana amene ukufunawo?’

      Kenako Hana ananyamuka kupita kukapemphera. Iye anapempha Yehova kuti amuthandize ndipo ankapemphera uku akulira. Hana analonjeza kuti: ‘Yehova, mukandipatsa mwana wamwamuna ndidzakupatsani kuti azikutumikirani kwa moyo wake wonse.’

      Eli yemwe anali Mkulu wa Ansembe akuona Hana akupemphera uku akulira

      Mkulu wa ansembe dzina lake Eli ataona milomo ya Hana ikugwedera, anaganiza kuti waledzera. Koma Hana anayankha kuti: ‘Ayi, mbuyanga, inetu sindinaledzere. Ndili ndi vuto lalikulu kwambiri limene ndikufotokozera Yehova.’ Eli anazindikira kuti walakwitsa ndipo anauza Hanayo kuti: ‘Mulungu akupatse zimene ukufunazo.’ Zitatero Hana anayamba kumva bwino mumtima ndipo anabwerera. Chaka chisanathe, anabereka mwana n’kumupatsa dzina loti Samueli. Iye ayenera kuti anasangalala kwambiri.

      Hana sanaiwale zimene analonjeza kwa Yehova. Samueli atangosiya kuyamwa, anamupereka kuti azikatumikira kuchihema. Iye anauza Eli kuti: ‘Mwana uyu ndi amene ndinkapempha nthawi ijayi. Ndamupereka kuti atumikire Yehova kwa moyo wake wonse.’ Chaka chilichonse, Elikana ndi Hana ankapita kukaona Samueli ndipo ankamutengera malaya atsopano odula manja. Yehova anapatsa Hana ana ena, aamuna atatu ndi aakazi awiri.

      “Pitirizani kupempha ndipo adzakupatsani. Pitirizani kufunafuna ndipo mudzapeza.”​—Mateyu 7:7

      Mafunso: N’chifukwa chiyani Hana anakhumudwa kwambiri? Kodi Yehova anadalitsa bwanji Hana?

      1 Samueli 1:1-28; 2:1-11, 18-21

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena