-
Nyumba ya YehovaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 44
Nyumba ya Yehova
Solomo atakhala mfumu ya Isiraeli, Yehova anamufunsa kuti: ‘Kodi ukufuna ndikupatse chiyani?’ Solomo anayankha kuti: ‘Ndine mwana ndipo sindikudziwa zambiri. Ndipatseni nzeru kuti ndizitha kulamulira bwino anthu anu.’ Yehova anamuyankha kuti: ‘Popeza wandipempha nzeru, ndipangitsa kuti ukhale munthu wanzeru kuposa wina aliyense. Koma ndikupatsanso chuma. Ndipo ukamandimvera, udzakhala ndi moyo wautali.’
Kenako Solomo anayamba kumanga nyumba ya Yehova. Anagwiritsa ntchito golide, siliva, mitengo komanso miyala ndipo zonsezi zinali zamtengo wapatali. Panali amuna ndi akazi aluso amene ankagwira ntchito yomanga nyumbayo. Patadutsa zaka 7 ntchito yomangayi inatha ndipo inali nthawi yoti nyumbayo aipereke kwa Yehova. Nyumbayi inali ndi guwa pomwe anaikapo nsembe. Solomo anagwada patsogolo pa guwalo n’kupemphera kuti: ‘Yehova, nyumbayi si yokongola kwambiri komanso si yaikulu kwambiri moti inu n’kukwanamo. Koma tiloleni kuti tizikulambirani m’nyumbayi ndipo muzimva mapemphero athu.’ Kodi Yehova anamva bwanji ndi zimene Solomo ananena m’pempheroli? Solomo atangomaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba n’kupsereza nsembe zonse zimene zinali paguwa zija. Izi zinasonyeza kuti Yehova anasangalala ndi nyumbayi ndipo Aisiraeli ataona zimenezi, anasangalala kwambiri.
Mfumu Solomo ankadziwika mu Isiraeli monse komanso m’madera akutali kuti anali wanzeru. Anthu ankabwera kwa iye kuti adzawathandize pa mavuto awo. Nayonso mfumukazi ya ku Seba inabwera kudzamuyesa pomufunsa mafunso ovuta. Koma itamva mayankho a Solomo inati: ‘Sindinkakhulupirira zimene anthu anandiuza zokhudza inu. Koma panopa ndaona kuti mulidi ndi nzeru kwambiri kuposanso mmene anthuwo ankafotokozera. Yehova Mulungu wanu wakudalitsani kwambiri.’ Zonse zinkayenda bwino ku Isiraeli ndipo anthu ankasangalala. Koma patapita nthawi zinthu zinasintha.
“Tsopano wina woposa Solomo ali pano.”—Mateyu 12:42
-
-
Ufumu UnagawikanaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 45
Ufumu Unagawikana
Pamene Solomo ankalambira Yehova, ku Isiraeli kunali mtendere. Koma kenako anakwatira akazi ambiri a mitundu ina ndipo akaziwa ankalambira mafano. Pang’ono ndi pang’ono, Solomo anasintha ndipo nayenso anayamba kulambira mafano. Yehova anakwiya kwambiri ndi zimenezi. Ndiyeno anauza Solomo kuti: ‘Ufumu wa Isiraeli uchotsedwa ku banja lako ndipo ugawikana pawiri. Ndidzapereka mbali yaikulu ya ufumuwu kwa mtumiki wako ndipo banja lako lidzatsala ndi mbali yochepa.’
Yehova anachitanso zinthu zina posonyeza kuti zimenezi zidzachitikadi. Tsiku lina, mtumiki wina wa Solomo dzina lake Yerobowamu anali pa ulendo ndipo anakumana ndi mneneri Ahiya. Ahiya anang’amba chovala chake zidutswa zokwana 12. Atatero anauza Yerobowamu kuti: ‘Yehova achotsa ufumu wa Isiraeli ku banja la Solomo ndipo augawa pawiri. Tenga zidutswa 10 izi chifukwa iweyo udzakhala mfumu ya mafuko 10.’ Mfumu Solomo atamva zimenezi, ankafuna kupha Yerobowamu. Choncho Yerobowamu anathawira ku Iguputo. Patapita nthawi, Solomo anamwalira ndipo mwana wake Rehobowamu anakhala mfumu. Zitatero Yerobowamu anaona kuti akhoza kubwerera ku Isiraeli.
Akuluakulu a ku Isiraeli anauza Rehobowamu kuti: ‘Mukamawalamulira bwino anthuwa, akhala okhulupirika kwa inu.’ Koma achinyamata anzake anamuuza kuti: ‘Anthuwa musamawalamulire mowanyengerera. Muziwagwiritsa ntchito zolemetsa kuposa zimene bambo anu ankawagwiritsa.’ Rehobowamu anamvera malangizo amenewa. Choncho ankalamulira anthuwo mwankhanza ndipo iwo anamuukira. Anthuwo anasankha Yerobowamu kuti akhale mfumu ya mafuko 10, omwe ankadziwika kuti ufumu wa Isiraeli. Mafuko awiri okha ndi amene anakhalabe okhulupirika kwa Rehobowamu ndipo ankadziwika kuti ufumu wa Yuda. Apa ndiye kuti mafuko 12 a Aisiraeli anagawikana.
Yerobowamu sankafuna kuti anthu ake azipita kukalambira ku Yerusalemu kumene mfumu yake anali Rehobowamu. Kodi ukudziwa chifukwa chake? Yerobowamu ankaopa kuti anthuwo akhoza kumuukira n’kupita kumbali ya Rehobowamu. Choncho anapanga mafano awiri a ana a ng’ombe n’kuuza anthuwo kuti: ‘Muzilambirira konkuno, chifukwatu ku Yerusalemu n’kutali.’ Ndiye anthuwo anayambadi kulambira ana a ng’ombewo ndipo anaiwala Yehova.
“Musamangidwe mʼgoli ndi osakhulupirira, chifukwa ndinu osiyana. Pali mgwirizano wotani pakati pa chilungamo ndi kusamvera malamulo? . . . Nanga munthu wokhulupirira ndi wosakhulupirira angafanane pa zinthu ziti?”—2 Akorinto 6:14, 15
-