NYIMBO 90
Tizilimbikitsana
Losindikizidwa
1. Pomwe tikulimbikitsana
Kutumikira Yehova,
Chikondi chathu chimakula
Ndipo timagwirizana.
Chikondi cha anthu a M’lungu
N’chothandiza kupirira.
Timatetezedwa kwambiri
Tikamakhala mumpingo.
2. Mawu a pa nthawi yabwino
Amatilimbikitsadi.
Mawu otilimbikitsawa
Amachoka kwa abale.
Kugwirira ntchito limodzi
Kumatigwirizanitsa.
Tizikhala olimbikitsa
Ndipo tizithandizana.
3. Pamene tsiku la Yehova
Layandikira kwambiri,
Tipitirize kusonkhana
Kuti tiyende ndi M’lungu.
Tigwirizane ndi abale,
Titumikire limodzi.
Choncho tizilimbikitsana
Kuti tikhulupirike.
(Onaninso Luka 22:32; Mac. 14:21, 22; Agal. 6:2; 1 Ates. 5:14.)