Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • sjj nyimbo 96
  • Baibulo Ndi Chuma

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Baibulo Ndi Chuma
  • Imbirani Yehova Mosangalala
  • Nkhani Yofanana
  • Buku la Mulungu Ndi Chuma Chamtengo Wapatali
    Imbirani Yehova
  • Bukhu la Mulungu—Chuma
    Imbirani Yehova Zitamando
  • Kuyamikira Kudekha kwa Mulungu
    Imbirani Yehova Zitamando
  • Bwerani kwa Mulungu Kuti Mupulumuke
    Imbirani Yehova Mosangalala
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Mosangalala
sjj nyimbo 96

NYIMBO 96

Baibulo Ndi Chuma

Losindikizidwa

(Miyambo 2:1)

  1. 1. Pali buku limene mawu ake

    Amatibweretsera chimwemwe.

    Mfundo zake zodabwitsa n’zamphamvu,

    Limapatsa nzeru owerenga.

    Bukuli ndi Baibulo loyera.

    Olilemba anauziridwa.

    Ankakonda Yehova M’lungu wawo,

    Mzimu wake unawathandiza.

  2. 2. Analemba zokhudza chilengedwe,

    Mmene M’lungu anachilengera.

    Analembanso za Paradaiso

    Ndiponso za mmene anathera.

    Analemba za mngelo winawake

    Amene ananyoza Yehova.

    Anabweretsa mavuto pa anthu

    Koma Yehova adzapambana.

  3. 3. Masiku ano tikusangalala

    Ufumu wa Mulungu wayamba.

    Tiuze anthu uthenga wabwino

    Ndi madalitso omwe abwere.

    M’Baibulo muli zosangalatsa.

    Chakudya chochuluka kwambiri.

    Limatipatsa mtendere wambiri,

    Tiyesetse kumaliwerenga.

(Onaninso 2 Tim. 3:16; 2 Pet. 1:21.)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena