Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 11/12 tsamba 12-15
  • Baibulo Ndi Buku la Maulosi Olondola Gawo 7

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Baibulo Ndi Buku la Maulosi Olondola Gawo 7
  • Galamukani!—2012
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Mulungu Athetsa Zoipa Zonse
  • Maulosi a M’Baibulo Ndi Odalirika
  • Kodi Babulo Wamkulu N’chiyani?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Ufumu Ukulamulira
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
  • Kodi “Babulo Wamkulu” N’chiyani?
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Maulosi Amene Anakwaniritsidwa
    Baibulo—Kodi Ndilo Mawu a Mulungu Kapena a Munthu?
Onani Zambiri
Galamukani!—2012
g 11/12 tsamba 12-15

Baibulo Ndi Buku la Maulosi Olondola Gawo 7

“Mapeto Adzafika”

Nkhani zokwanira 8 zimene zikhale zikutuluka mu Galamukani!, zizifotokoza maulosi osiyanasiyana a m’Baibulo. Nkhanizi zikuthandizani kupeza mayankho a mafunso awa: Kodi maulosi a m’Baibulo analembedwa ndi anthu kapena pali umboni wakuti analembedwa ndi Mulungu? Kuwerenga nkhanizi kukuthandizani kudziwa zoona zenizeni.

KODI zimakupwetekani mukamaona maboma ankhanza akupondezera komanso kudyera masuku pamutu nzika zawo? Kodi mumaona kuti sichilungamo kuti makampani akuluakulu azibera anthu osauka n’cholinga cholemeretsa anthu omwe ali kale ndi ndalama zambiri? Kapena kodi zimakuwawani kuona atsogoleri achipembedzo akubera anthu a m’zipembedzo zawo komanso kuwaphunzitsa zabodza? Dziwani kuti Baibulo limasonyeza kuti Mulungu amadana ndi makhalidwe oipa amenewa. M’nkhani ino tikambirana (1) Maulosi a m’Baibulo osonyeza kuti Mulungu athetsa zoipa zonse ndi kuwononga anthu onse oipa ndiponso (2) Chifukwa chake sitiyenera kukayikira maulosi amenewa.

Mulungu Athetsa Zoipa Zonse

Nkhani ya nambala 6 ya nkhani zino, inafotokoza za chizindikiro cha mbali zingapo chimene Yesu ananena chosonyeza kuti mapeto ayandikira. Mbali imodzi ya chizindikirochi ndi kulalikidwa kwa uthenga wabwino wonena za Ufumu wa Mulungu. Ufumu umenewu ndi boma la Mulungu lomwe posachedwapa liyamba kulamulira dziko lapansi. (Danieli 2:44; Mateyu 24:3, 14) Yesu ananena kuti ntchito yolalikira uthenga umenewu ikadzatha, “mapeto adzafika.” Mungadabwe kudziwa kuti chinthu choyamba chimene Mulungu adzawononge ndi chipembedzo chonyenga, chomwe chimaphunzitsa zinthu zabodza zokhudza Mulunguyo. M’Baibulo, chipembedzo chonyenga amachiyerekezera ndi hule lalikulu lomwe ndi “Babulo Wamkulu.”​—Chivumbulutso 17:1, 5; onani bokosi lakuti “Kodi Tingamudziwe Bwanji Babulo Wamkulu?” patsamba 13.

Ulosi woyamba:

“Miliri idzafika [pa Babulo Wamkulu]. Miliri yakeyo ndiyo imfa, kulira, ndi njala. Ndipo adzanyekeratu ndi moto chifukwa Yehova Mulungu, amene anamuweruza, ndi wamphamvu.”​—Chivumbulutso 18:2, 8.

Kukwaniritsidwa kwake: Baibulo limasonyeza kuti Mulungu anasankha nthawi yoti adzachititse maboma apadziko lapansi kuukira Babulo Wamkulu n’kumuwononga. Limanena kuti mabomawa ‘adzamusakaza ndi kumusiya wamaliseche ndipo adzadya minofu yake.’ (Chivumbulutso 17:16) Zimenezi zikutanthauza kuti mabomawo adzaonetsa poyera zinthu zochititsa manyazi zimene huleli limachita ndipo adzalilanda chuma chake. Babulo Wamkulu adzawonongedwa mofulumira ndipo sipadzatsala chilichonse chosonyeza kuti analipo.​—Chivumbulutso 18:21.

Nthawi imeneyo mabomawa azidzaona ngati iwowo aganiza okha zowononga Babulo Wamkulu. Koma zimene zidzachitike n’zimene zidzasonyeze kuti Mulungu ndi amene wachititsa kuti Babulo Wamkulu awonongedwe. Ponena za kuwonongedwa kwa Babulo Wamkulu, Baibulo limati, Mulungu adzaika ‘izi [maganizo owononga Babulo Wamkulu] m’mitima yawo [maboma] kuti achite monga mwa maganizo ake.’​—Chivumbulutso 17:17.

Ulosi wachiwiri:

“M’masiku a mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu. . . . Ufumuwo . . . udzaphwanya ndi kuthetsa maufumu ena onsewo, [maboma a anthu] ndipo udzakhalapo mpaka kalekale.”​—Danieli 2:44.

Kukwaniritsidwa kwake: Mulungu akadzathana ndi chipembedzo chonyenga, adzawononganso mabungwe onse andale, amalonda komanso anthu onse ochita zoipa. (Miyambo 2:22; Chivumbulutso 19:17, 18) Mofanana ndi mwininyumba amene akuchotsa walendi woipa, Mulungu adzawononga anthu “amene akuwononga dziko lapansi.” Adzawononga anthu onse omwe amachita makhalidwe oipa monga chiwawa komanso chiwerewere.​—Chivumbulutso 11:18; Aroma 1:18, 26-29.

Ndiye kodi ndani amene adzapulumuke? Baibulo limayankha kuti: “Ofatsa adzalandira dziko lapansi, ndipo adzasangalala ndi mtendere wochuluka.”​—Salimo 37:11; 72:7.

Kodi pali zifukwa zokhulupirira maulosi a m’Baibulo? Kodi pali zifukwa zomveka zokhulupirira kuti Mulungu adzathetsadi mavuto komanso zoipa zonse ndiponso kuti adzapulumutsa anthu olungama? Inde zilipo.

Maulosi a M’Baibulo Ndi Odalirika

A Mboni za Yehova amakhulupirira kuti Yehova Mulungu ndi amene analemba Baibulo komanso kuti adzachita zonse zimene analonjeza. (2 Timoteyo 3:16) Kodi pali chifukwa chokhulupirira zimenezi?

Tiyerekeze kuti muli ndi mnzanu yemwe munayamba kugwirizana naye kalekale ndipo amakukondani komanso sanayambepo wakunamizani. Ngati mnzanuyo wakulonjezani kuti akuchitirani zinazake zabwino ndipo mukudziwa kuti ali ndi mphamvu zochitira zimene walonjezazo, kodi mungamukayikire? N’zachidziwikire kuti simungamukayikire. Mulungu ndi wokhulupirika ndipo amakwaniritsa zonse zimene walonjeza kuposa mnzanu aliyense amene mungakhale naye. Baibulo limati Mulungu “sanganame.”—Tito 1:2.

N’zoonadi kuti Mlengi wathu adzawononga chipembedzo chonyenga, maboma opondereza komanso amalonda omwe amadyera anthu masuku pamutu. Kodi mungafune kudziwa zina zimene zidzachitike Mulungu akadzachita zimenezi? M’magazini yotsatira mudzakhala nkhani yomalizira ya nkhani zimenezi ndipo idzafotokoza zimene zidzachitike.

KODI TINGAMUDZIWE BWANJI BABULO WAMKULU?

Kodi tingadziwe bwanji kuti mkazi wotchedwa Babulo Wamkulu, yemwe amamutchula m’buku la Chivumbulutso, amaimira chipembedzo chonyenga? Taonani umboni wotsatirawu:

  • Mkazi ameneyu sangakhale munthu chifukwa buku la Chivumbulutso limafotokoza zinthu mwa “zizindikiro” kapena kuti mophiphiritsira.​—Chivumbulutso 1:1.

  • Babulo Wamkulu wakhala pamadzi ambiri ndipo madzi amenewa akuimira “mitundu ya anthu, makamu [ndi] mayiko.” (Chivumbulutso 17:1, 5, 15) Munthu weniweni sangathe kuchita zimenezi. Choncho Babulo Wamkulu akuimira chipembedzo chonyenga chomwe chimathandizidwa ndi anthu ochuluka.

  • Mkazi ameneyu akuimira “mzinda waukulu umene ukulamulira mafumu a dziko lapansi.” M’mawu ena, mkazi ameneyu ndi gulu ndipo lili ndi mphamvu pa dziko lonse.​—Chivumbulutso 17:18.

  • Huleli silingakhale mafumu a dziko lapansi omwe ndi andale. Baibulo limanena kuti hule lophiphiritsira limeneli, lomwe ndi Babulo Wamkulu, lapanga mgwirizano ndi “mafumu a dziko lapansi.” Ndipo mafumu amenewa adzalira hule limeneli likadzawonongedwa.​—Chivumbulutso 17:1, 2; 18:9.

  • Huleli silingakhalenso amalonda chifukwa amalondawo adzamulira akadzawonongedwa.​—Chivumbulutso 18:15.

  • Baibulo limanena kuti anthu amene amalambira Mulungu n’kumakondanso za m’dziko, akuchita chigololo. (Yakobo 4:4) Zimenezi ndi zimene Babulo Wamkulu amachita. Komanso amachita zamizimu polambira.​—Chivumbulutso 18:23.

  • Anthu a mumzinda wakale wa Babulo, umene dzina lakuti Babulo Wamkulu linachokera, ankakonda kwambiri zopembedza.​—Yesaya 47:1, 12, 13; Yeremiya 50:1, 2, 38.

Choncho tinganene motsimikiza kuti Babulo Wamkulu akuimira zipembedzo zonse zonyenga.

MAULOSI A M’BAIBULO OMWE ANAKWANIRITSIDWA

M’munsimu muli maulosi a m’Baibulo ochititsa chidwi amene anafotokozedwa m’nkhani 6 zoyambirira. Nkhani zimenezi zinasonyeza kuti maulosi amenewa anakwaniritsidwa ndipo ena akukwaniritsidwa panopo.

MAULOSI ONENA ZA ABULAHAMU NDI MBADWA ZAKE

  • Mbadwa za Abulahamu yemwe anali wokhulupirika, zidzakhala mtundu waukulu womwe udzadziwike kuti mtundu wa Isiraeli.​—Genesis 12:1, 2.

  • Mbadwa za Abulahamu zidzabwerera kudziko la Kanani zitakhala m’dziko la eni kwa zaka 400.​—Genesis 15:13, 16.

  • Mbadwa za Abulahamu zidzalanda “dziko lonse la Kanani.”​—Genesis 17:8.

  • Mulungu adzalola kuti Aisiraeli agonjetsedwe n’kutengedwa ku ukapolo chifukwa chosamumvera.​—Yeremiya 25:8-11.

  • Mulungu adzabwezeretsa Ayuda kudziko lakwawo, atakhala ku ukapolo kwa zaka 70.​—Yeremiya 25:12; 29:10.

  • Ufumu wa Babulo womwe unkalamulira padziko lonse udzagonjetsedwa ndipo mzinda wa Babulo udzakhala bwinja.​—Yesaya 13:19, 20.

MAULOSI ONENA ZA MESIYA NDI OTSATIRA AKE

  • Mesiya kapena kuti Khristu, adzakhala mbadwa ya Mfumu Davide.​—Yesaya 9:7.

  • Mesiya adzabadwira ku Betelehemu.​—Mika 5:2.

  • Mesiya adzaonekera patatha zaka 483, “kuchokera pamene mawu adzamveka onena kuti Yerusalemu akonzedwe ndi kumangidwanso.” Lamulo limeneli linaperekedwa mu 455 B.C.E.​—Danieli 9:25.

  • Asanaphedwe, Mesiya adzakwapulidwa mwankhanza​.—Yesaya 50:6.

  • Mesiya adzaphedwa ngati munthu wophwanya malamulo koma adzaikidwa m’manda limodzi ndi “anthu olemera.”​—Yesaya 53:9.

  • Otsatira a Khristu adzafalitsa uthenga wabwino ku Yudeya, ku Samariya ndi kumadera onse.​—Machitidwe 1:8.

  • Akhristu adzazunzidwa.​—Maliko 13:9.

  • Anthu achinyengo komanso opondereza adzalowa mumpingo wachikhristu, n’kuyamba kupatutsa anthu ena kuti aziwatsatira.​—Machitidwe 20:29, 30; 2 Petulo 2:1, 2.

MAULOSI ONENA ZA MASIKU OTSIRIZA

M’masiku otsiriza kudzachitika zotsatirazi:

  • “Uthenga wabwino . . . wa ufumu [wa Mulungu]” udzalalikidwa padziko lonse.​—Mateyu 24:14.

  • Nkhondo padziko lonse.​—Mateyu 24:7; Chivumbulutso 6:4.

  • Njala.​—Mateyu 24:7.

  • Zivomezi.​—Luka 21:11.

  • Miliri.​—Luka 21:11.

  • Chidani komanso chiwawa.​—Mateyu 24:10, 12.

  • Anthu adzakhala adyera, odzikonda komanso okonda ndalama.​—2 Timoteyo 3:1-5.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena