Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w16 August tsamba 30
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Chilamulo Kristu Asanadze
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Kodi Chimaipitsa Munthu N’chiyani?
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Kodi Chimaipitsa Munthu Nchiyani?
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Nchiyani Chiipitsa Munthu?
    Nsanja ya Olonda—1987
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
w16 August tsamba 30
Mfarisi akusamba m’manja mwamwambo ndipo akuyang’ana moweruza munthu amene wayamba kale kudya

Mafunso Ochokera Kwa Owerenga

N’chifukwa chiyani anthu amene ankatsutsa Yesu ankaona kuti kusamba m’manja ndi nkhani yaikulu?

Yesu ndi ophunzira ake ankatsutsidwa pa nkhani imeneyi komanso nkhani zina. Chilamulo cha Mose chinkafotokoza zinthu zimene zingachititse munthu kukhala wodetsedwa. Zinthu zake zinali monga matenda akukha, matenda akhate komanso kukhudza mtembo wa munthu kapena wa nyama. Chilamulocho chinkafotokozanso zimene munthu angachite kuti ayeretsedwe. Ankafunika kupereka nsembe, kusamba komanso kuwaza madzi kapena magazi.—Levitiko chaputala 11-15; Numeri chaputala 19.

Koma Afarisi ankakokomeza malamulo okhudza nkhani imeneyi. Buku lina linanena kuti iwo anakhazikitsa malamulo ambirimbiri otchula zinthu zimene zingachititse munthu kukhala wodetsedwa komanso kudetsa anzake. Ankanenanso za zipangizo zimene zingadetse anthu komanso miyambo imene ayenera kuchita kuti ayeretsedwe.

Pa nthawi ina anthu amene ankadana ndi Yesu anamufunsa kuti: “N’chifukwa chiyani ophunzira anu satsatira miyambo ya makolo, koma amadya chakudya ndi manja oipitsidwa?” (Maliko 7:5) Apa sikuti ankangonena zosamba m’manja chifukwa cha ukhondo. Koma ankanena za mwambo umene ankachita pothirirana madzi asanayambe kudya. Buku lija linanenanso kuti iwo anakhazikitsa malamulo onena za madzi oyenera, chotungira choyenera, munthu woyenera kukuthirira madziwo komanso kuti munthu azisamba m’manja kufika muti.

Yesu sanavutike poyankha anthuwo. Iye anangowauza kuti: “Yesaya analosera moyenera za anthu onyenga inu, monga mmene Malemba amanenera kuti, ‘Anthu awa amandilemekeza ndi milomo yokha, koma mitima yawo ili kutali ndi ine [Yehova]. Amandipembedza pachabe, chifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati ziphunzitso za Mulungu.’ Mumanyalanyaza malamulo a Mulungu, ndi kuumirira mwambo wa anthu.”—Maliko 7:6-8.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena