LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 1
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Mawu opita kwa Teofilo (1-5)

      • Kucitila umboni mpaka kumalekezelo a dziko lapansi (6-8)

      • Yesu apita kumwamba (9-11)

      • Ophunzila asonkhana pamodzi mogwilizana (12-14)

      • Matiya asankhidwa kuti alowe m’malo Yudasi (15-26)

Macitidwe 1:6

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, masa. 35-36

Macitidwe 1:8

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “mpaka kumadela a kutali kwambili.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 21

    Nsanja ya Mlonda,

    7/15/2014, masa. 29-30

Macitidwe 1:12

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “Mtunda wa pa tsiku la Sabata.” Uyu ndi mtunda umene Myuda anali kuloledwa kuyenda pa Sabata.

Macitidwe 1:14

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    8/15/2015, tsa. 30

Macitidwe 1:15

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “Khamu lonse linali pafupifupi anthu 120.”

Macitidwe 1:18

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “anaphulika pakati.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 1:1-26

Macitidwe a Atumwi

1 A Teofilo, m’buku loyamba, ndinalemba zonse zimene Yesu anacita ndi kuphunzitsa 2 mpaka tsiku limene iye anatengedwa kupita kumwamba, pambuyo pakuti wapeleka malangizo kupyolela mwa mzimu woyela kwa atumwi amene anasankha. 3 Yesu atazunzika mpaka imfa, anaonekela kwa iwo ali wamoyo mwa kugwilitsa nchito maumboni okhutilitsa. Kwa masiku 40, iye anaonekela kwa iwo nthawi zambili, ndipo anali kukamba nawo za Ufumu wa Mulungu. 4 Pa nthawi imene anasonkhana nawo pamodzi, anawalangiza kuti: “Musacoke mu Yerusalemu, koma pitilizani kuyembekezela lonjezo la Atate limene munamva kwa ine. 5 Cifukwa Yohane anali kubatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi mzimu woyela pasanapite masiku ambili.”

6 Conco atasonkhana pamodzi, anamufunsa kuti: “Ambuye kodi mubwezeletsa ufumu kwa Aisiraeli pa nthawi ino?” 7 Iye anawayankha kuti: “Si kwa inu kudziwa nthawi kapena nyengo imene Atate asankha mu ulamulilo wawo. 8 Mzimu woyela ukadzafika pa inu, mudzalandila mphamvu, ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka kumalekezelo* a dziko lapansi.” 9 Atatsiliza kukamba zimenezi, anatengedwa kupita kumwamba iwo akuona, ndipo mtambo unamuphimba cakuti sanathenso kumuona. 10 Ndipo pamene iwo anali kuyang’anitsitsa kumwamba pomwe iye anali kupita, mwadzidzidzi amuna awili ovala zoyela anaimilila pambali pawo. 11 Amunawo anati: “Amuna inu a mu Galileya, n’cifukwa ciyani mwangoimilila n’kumayang’ana kumwamba? Yesu amene watengedwa pakati panu kupita kumwamba, adzabwela mofanana ndi mmene mwamuonela akupita kumwamba.”

12 Ndiyeno iwo anabwelela ku Yerusalemu kucoka kuphili lochedwa Phili la Maolivi limene linali pafupi ndi Yerusalemu, pa mtunda wa pafupifupi kilomita imodzi* kucokela ku Yerusalemu. 13 Iwo atafika kumeneko, anapita m’cipinda cam’mwamba mmene anali kukhala. Mmenemo munali Petulo, Yohane, Yakobo, Andireya, Filipo, Tomasi, Batolomeyo, Mateyo, Yakobo mwana wa Alifeyo, Simoni wochedwanso kuti wakhama, komanso Yudasi mwana wa Yakobo. 14 Onsewa mogwilizana anali kulimbikila kupemphela pamodzi ndi Mariya mayi ake a Yesu, azimayi ena, komanso abale ake a Yesu.

15 M’masiku amenewo, Petulo anaimilila pakati pa abalewo (ciwelengelo* ca anthu onse cinali pafupifupi 120) ndipo anati: 16 “Amuna inu, abale, kunali kofunikila kuti lemba likwanilitsidwe limene mzimu woyela unanenelatu kudzela mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolela anthu kuti agwile Yesu. 17 Iye anali pakati pathu, ndipo anatengako mbali pa utumiki umenewu. 18 (Munthu ameneyu, anagula munda ndi malipilo a nchito zosalungama. Iye anagwa camutu, ndipo thupi lake linaphulika* moti matumbo ake anakhutuka. 19 Nkhani imeneyi inadziwika kwa anthu onse okhala mu Yerusalemu, moti m’cinenelo cawo mundawo anaucha kuti A·kel′da·ma, kutanthauza “Munda wa Magazi.”) 20 Pakuti m’buku la Masalimo analembamo kuti, ‘Malo ake okhala akhale matongwe, ndipo pasapezeke aliyense wokhalapo,’ ndiponso kuti ‘Udindo wake monga woyang’anila, munthu wina autenge.’ 21 Conco m’pofunika kuti iye alowedwe m’malo ndi mmodzi wa amuna amene anali kuyenda nafe pa nthawi yonse imene Ambuye Yesu anali kucita utumiki wawo pakati pathu. 22 Munthu ameneyo, akhale amene anali kuyenda nafe kuyambila pamene Yesu anabatizidwa ndi Yohane, mpaka tsiku limene anatengedwa pakati pathu kupita kumwamba. Munthuyo ayenela kukhala mboni ya kuukitsidwa kwake pamodzi ndi ife.”

23 Conco, panachulidwa amuna awili, Yosefe wochedwa Barasaba amene analinso kuchedwa kuti Yusito, ndi Matiya. 24 Ndiyeno anapemphela kuti: “Inu Yehova, mumadziwa mitima ya anthu onse, tionetseni amene mwasankha pakati pa amuna awiliwa 25 kuti atenge malo a utumikiwu ndi kukhala mtumwi, zimene Yudasi anasiya n’kuyenda njila zake.” 26 Conco iwo anacita maele, ndipo maelewo anagwela Matiya. Cotelo iye anawonjezedwa pa atumwi 11 aja.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani