Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
16 “Ndakuuzani zinthu zimenezi kuti musataye* cikhulupililo canu. 2 Anthu adzakucotsani m’sunagoge. Ndipo nthawi idzafika pamene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti wacita utumiki wopatulika kwa Mulungu. 3 Koma adzacita zinthu zimenezi cifukwa Atate sawadziwa komanso ine sandidziwa. 4 Komabe, ndakuuzani zinthu zimenezi kuti nthawi yakuti zicitike ikadzafika, mukakumbukile kuti ndinakuuzani.
“Poyamba sindinakuuzeni zinthu zimenezi cifukwa ndinali nanu. 5 Tsopano ndikupita kwa amene anandituma, koma palibe ngakhale mmodzi wa inu amene wandifunsa kuti, ‘Mukupita kuti?’ 6 Koma cifukwa ndakuuzani zinthu zimenezi, mitima yanu yadzala ndi cisoni. 7 Kukuuzani zoona, kupita kwanga kudzakupindulilani. Cifukwa ngati sindingapite, mthandizi uja sadzabwela kwa inu. Koma ndikapita ndidzamutumiza kwa inu. 8 Ndipo iye akadzabwela, adzapeleka umboni wokhutilitsa kudzikoli wonena za ucimo, cilungamo, komanso ciweluzo. 9 Coyamba adzapeleka umboni wokamba za ucimo, cifukwa iwo sakundikhulupilila. 10 Kenako adzapeleka umboni wokamba za cilungamo, cifukwa ndikupita kwa Atate ndipo inu simudzandionanso. 11 Pamapeto pake, adzapeleka umboni wokamba za ciweluzo, cifukwa wolamulila wa dzikoli waweluzidwa.
12 “Ndikali ndi zambili zakuti ndikuuzeni, koma simungazimvetse pali pano. 13 Koma mthandiziyo akadzabwela, amene ndi mzimu wa coonadi, adzakutsogolelani m’coonadi conse. Pakuti iye sadzalankhula zongoganiza pa iye yekha, koma adzalankhula zimene wamva ndipo adzalengeza kwa inu zinthu zimene zidzabwela. 14 Ameneyo adzandilemekeza, cifukwa adzalengeza kwa inu zimene adzalandila kucokela kwa ine. 15 Zinthu zonse zimene Atate ali nazo ndi zanga. Ndiye cifukwa cake ndanena kuti mthandiziyo adzalengeza zimene walandila kucokela kwa ine. 16 Kwa kanthawi kocepa simudzanionanso, ndipo kwa kanthawi kocepa mudzandiona.”
17 Atakamba zimenezi, ena mwa ophunzila ake anayamba kufunsana kuti: “Kodi watanthauzanji potiuza kuti, ‘Kwa kanthawi kocepa simudzandionanso, ndipo kwa kanthawi kocepa mudzandiona,’ komanso kuti, ‘cifukwa ndikupita kwa Atate’?” 18 Iwo anali kukamba kuti: “Kodi akutanthauza ciyani ponena kuti, ‘kwa kanthawi kocepa’? Sitikumvetsa zimene akukamba.” 19 Yesu anadziwa kuti iwo anali kufuna kumufunsa. Conco anawauza kuti: “Kodi mukufunsana zimenezi cifukwa ndakamba kuti: ‘Kwa kanthawi kocepa simudzandionanso, ndipo kwa kanthawi kocepa mudzandiona’? 20 Ndithudi ndikukuuzani, inu mudzalila ndi kubuma,* koma dzikoli lidzakondwela. Mudzamva cisoni, koma cisoni canu cidzasanduka cimwemwe. 21 Mkazi pobeleka amavutika kwambili cifukwa nthawi yake yakwana. Koma akabeleka mwana, amaiwala zopwetekazo cifukwa ca cimwemwe cakuti munthu wabadwa padziko lapansi. 22 Cimodzimodzi inunso, pali pano muli ndi cisoni, koma ndidzakuonaninso ndipo mitima yanu idzakondwela. Palibenso amene adzakulandani cimwemwe canuco. 23 Patsiku limenelo simudzandifunsanso funso lililonse. Ndithudi ndikukuuzani, ngati mungapemphe ciliconse kwa Atate m’dzina langa adzakupatsani. 24 Mpaka pano simunapemphepo ciliconse m’dzina langa. Pemphani ndipo mudzalandila kuti cimwemwe canu cisefukile.
25 “Ndakuuzani zinthu zimenezi m’mafanizo. Nthawi ikubwela pamene sindidzalankhulanso nanu m’mafanizo, koma ndidzakuuzani momveka bwino za Atate. 26 Patsikulo mudzapempha cinthu kwa Atate m’dzina langa. Pokamba izi, sinditanthauza kuti ndidzakupemphelani ayi. 27 Atatewo amakukondani, cifukwa munandikonda, ndipo munakhulupilila kuti ndinabwela monga woimilako Mulungu. 28 Ndinabwela m’dzikoli monga woimilako Atate wanga. Tsopano ndikucoka m’dzikoli, ndipo ndikupita kwa Atate.”
29 Ophunzila ake anati: “Ambuye, tsopano mukulankhula zomveka bwino cifukwa simukugwilitsa nchito mafanizo. 30 Tsopano tadziwa kuti mumadziwa zinthu zonse, ndipo m’posafunikilanso kuti wina akufunseni mafunso. Mwa ici, tikukhulupilila kuti munacokela kwa Mulungu.” 31 Yesu anawafunsa kuti: “Kodi mwakhulupilila tsopano? 32 Taonani! Nthawi ikubwela, ndipo yafika kale, pamene nonse mudzabalalika aliyense kupita kunyumba kwake, ndipo mudzandisiya ndekha. Koma sindili ndekha, cifukwa Atate ali nane. 33 Ndakuuzani zinthu zimenezi, kuti kudzela mwa ine mukhale ndi mtendele. M’dzikoli mudzakumana ndi masautso, koma limbani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko.”