LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp16 na. 2 masa. 3-4
  • Kodi Zinacitikadi?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Zinacitikadi?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • ZIMENE MAUMBONI AKUONETSA
  • NANGA BWANJI ZA KUUKITSIDWA KWA YESU?
  • Kodi Kuukitsidwa kwa Yesu Kumatanthauza Ciani kwa Ife?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Akufa Adzauka Ndithu—Sitikaika Konse!
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • “Ine Ndili Ndi Ciyembekezo mwa Mulungu”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
wp16 na. 2 masa. 3-4
Thupi la Yesu licotsedwa pa mtengo wozunzikilapo pamene ophunzila ake akuyang’ana capatali

NKHANI YA PACIKUTO | N’CIFUKWA CIANI YESU ANAVUTIKA NDI KUTIFELA?

Kodi Zinacitikadi?

Mu 33 C.E., Yesu wa ku Nazareti anaphedwa. Iye anapatsidwa mlandu wabodza woukila boma, anamenyedwa mwankhanza, ndipo anakhomeledwa pamtengo. Iye anafa imfa yoŵaŵa. Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, ndipo patapita masiku 40 Yesu anabwelela kumwamba.

Zocitika zapadela zimenezi zinalembedwa m’mabuku anai a Uthenga Wabwino a m’Malemba Acigiliki Acikristu, amene amadziŵika kuti Cipangano Catsopano. Kodi zimene zinalembedwa m’mauthenga amenewo zinacitikadi? Funso limeneli n’lofunika kwambili. Ngati zinthu zimenezo sizinacitike, ndiye kuti cikhulupililo ca Akristu n’copanda nchito, ndipo ciyembekezo cokhala ndi moyo m’Paladaiso ndi loto cabe. (1 Akorinto 15:14) Komabe, ngati zinthuzo zinacitikadi, ndiye kuti anthu ali ndi tsogolo labwino kwambili, limene inu mungauzeko ena. Koma kodi nkhani za m’Mauthenga Abwino zinacitika kapena sizinacitike?

ZIMENE MAUMBONI AKUONETSA

Mosiyana ndi nthano zabodza, nkhani za m’Mauthenga Abwino zinafufuzidwa mosamala ndi kulembedwa molondola. Mwacitsanzo, zimachula maina a malo enieni, ndipo ambili mwa malo amenewa anthu angapite kukawaona masiku ano. Cina, zimafotokoza anthu enieni, ndipo akatswili olemba mbili yakale amacitila umboni kuti anthuwo analikodi.—Luka 3:1, 2, 23.

Olemba ena a m’nthawi ya atumwi komanso a m’zaka za m’ma 100 C.E., anachulapo za Yesu.a Njila imene Yesu anaphedwela yofotokozedwa m’Mauthenga Abwino ndi yofanana ndi njila zimene Aroma anali kugwilitsila nchito pakupha munthu. Kuonjezela apo, zocitika zimene analemba ndi zofanana m’njila yakuti zinalembedwa molondola ndiponso mosapita m’mbali. Iwo analembanso ngakhale zolakwa za ophunzila ena a Yesu. (Mateyu 26:56; Luka 22:24-26; Yohane 18:10, 11) Maumboni onsewa akuonetsa kuti olemba Mauthenga Abwino anali oona mtima, ndipo analemba zinthu zokhudza Yesu molondola kwambili.

NANGA BWANJI ZA KUUKITSIDWA KWA YESU?

Ngakhale kuti ambili amakhulupilila kuti Yesu anabweladi padziko lapansi kenako anaphedwa, ena amakaikila zakuti iye anaukitsidwa. Atumwi ake naonso sanakhulupilile pamene anamva lipoti lakuti iye waukitsidwa. (Luka 24:11) Komabe, pamene io ndi ophunzila ena anamuona Yesu woukitsidwayo panthawi zosiyanasiyana, m’pamene anakhulupilila. Ndipo panthawi ina, Yesu anaonekela kwa anthu oposa 500.—1 Akorinto 15:6.

Molimba mtima, ophunzila a Yesu analengeza za kuukitsidwa kwake kwa anthu ambili kuphatikizapo amene anamupha, ngakhale kuti kucita zimenezo kunaika moyo wao pangozi. (Machitidwe 4:1-3, 10, 19, 20; 5:27-32) Kodi ophunzila ambili akanalimba mtima conco zikanakhala kuti sanali otsimikiza mtima kuti Yesu anaukitsidwadi? Kukamba zoona, mfundo yakuti Yesu anaukitsidwadi ndi imene inacititsa kuti Cikristu cifalikile kwambili m’nthawi zakale ngakhale masiku ano.

Nkhani zokhudza imfa ya Yesu ndi kuukitsidwa kwake zolembedwa m’Mauthenga Abwino, ndi umboni wakuti nkhani zonse zofotokoza mbili yakale n’zoona. Kuŵelenga nkhani zimenezi bwinobwino, kudzakuthandizani kukhulupilila kuti zinacitikadi. Ndipo cikhulupililo canu cidzalimbanso mukamvetsetsa cifukwa cake zinthuzo zinacitika. Nkhani yotsatila ifotokoza zimenezi.

a Ena mwa anthu amenewa ndi Tacitus, amene anabadwa mu 55 C.E. Iye analemba kuti Akristu anatengela dzinali kwa “Kristu” amene Pontiyo Pilato, mmodzi mwa olamulila athu, anamulamula kuti azunzidwe ndi kuphedwa mu ulamulilo wa mfumu Tiberiyo.” Enanso amene analemba za Yesu anali Suetonius, (wa m’nthawi ya atumwi), wolemba mbili yakale waciyuda Josephus (wa m’nthawi ya atumwi), ndi Pliny Wamng’ono amene anali bwanamkubwa wa ku Bituniya (wa kumayambililo kwa zaka za m’ma 100 C.E).

N’cifukwa Ciani Pali Maumboni Ocepa Osakhala a m’Baibulo?

Ponena za mmene zocita za Yesu zinakhudzila anthu padziko lapansi, kodi tingayembekezele kupeza maumboni ena a m’nthawi ya atumwi kuposa a m’Baibulo, amene akuonetsa kuti Yesu anali munthu weniweni ndi kuti anaukitsidwa? Osati kwenikweni. Coyamba, Mauthenga Abwino analembedwa zaka pafupifupi 2,000 zapitazo. Ndipo zolemba zina za m’nthawi imeneyo zikalipo. (1 Petulo 1:24, 25) Ndiyeno, anthu ambili amene anali kutsutsa Yesu sakanalemba zinthu zimene zikanapangitsa anthu kukhulupilila Yesu.

Pankhani ya kuukitsidwa kwa Yesu, Petulo, amene anali mmodzi wa atumwi ake, anafotokoza kuti: “Ameneyu Mulungu anamuukitsa tsiku lacitatu ndi kumulola kuonekela, osati kwa anthu onse, koma kwa mboni zoikidwilatu ndi Mulungu, zomwe ndi ife amene tinadya ndi kumwa naye limodzi atauka kwa akufa.” (Machitidwe 10:40, 41) N’cifukwa ciani sanaonekele kwa anthu onse? Uthenga Wabwino wa Mateyu umatiuza kuti pamene atsogoleli acipembedzo amene anali adani a Yesu anamva kuti iye waukitsidwa, io anapeza njila yothetsela kufalitsidwa kwa nkhani yakuti Yesu wauka.—Mateyu 28:11-15.

Kodi izi zitanthauza kuti Yesu anali kufuna kuti nkhani yakuti iye anaukitsidwa isafalikile? Iyai. Petulo anapitiliza kufotokoza kuti: “Anatilamula kuti tilalikile kwa anthu ndi kupeleka umboni wokwanila wakuti iyeyu ndi amene Mulungu anamuika kukhala woweluza anthu amoyo ndi akufa.” Akristu oona akhala akucita zimenezi kuyambila kale.—Machitidwe 10:42.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani