LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp16 na. 4 tsa. 4
  • Baibulo Siinawole

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Baibulo Siinawole
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Nkhani Zofanana
  • Baibulo Inapulumuka kwa Anthu Ofuna Kusintha Uthenga Wake
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
wp16 na. 4 tsa. 4

NKHANI YA PACIKUTO | BAIBULO—MMENE YAPULUMUKILA

Baibulo Siinawole

VUTO LIMENE LINALIPO: Olemba Baibulo ndi okopela malemba, nthawi zambili anali kuseŵenzetsa gumbwa ndi zikopa (zikumba) za nyama.a (2 Timoteyo 4:13) Kodi zinthu zimenezi zikanapangitsa bwanji kuti Baibulo iwonongeke?

Gumbwa imang’ambika mosavuta, imasintha maonekedwe, ndipo imawonongeka. Akatswili odziŵa mbili ya ku Iguputo, Richard Parkinson ndi Stephen Quirke, anakamba kuti: “Gumbwa amawola mwamsanga ndi kusanduka dothi. Akasungidwa, akhoza kuwola ndi cinyontho kapena kudyewa ndi makoswe kapenanso tuzilombo twina, makamaka ciswe ngati amubisa m’nthaka.” Ofufuza anapeza kuti akaika gumbwa padzuŵa kapena pamalo a cinyontho, amawonongeka mofulumila.

Cikumba ca nyama n’colimba kupambana gumbwa, koma cimawonongeka ngati sicinasamalidwe bwino, kapena ngati caikidwa pamalo otentha kwambili, a cinyontho, kapena padzuŵa.b Cikumba naconso cimadyewa na tuzilombo. Ndiye cifukwa cake zolemba zambili zakale kulibe masiku ano. Baibulo ikanawonongeka, sembe uthenga wake kulibe.

MMENE BAIBULO INATETEZEKELA: M’cilamulo cimene Ayuda anapatsidwa, munali lamulo lakuti mfumu iliyonse iyenela “kukopela buku lakelake la Cilamulo,” kutanthauza mabuku asanu oyambilila a m’Baibulo. (Deuteronomo 17:18) Kuonjezela apo, okopela malemba aluso analemba mipukutu yambili cakuti pofika m’nthawi ya atumwi, Malemba anali kupezeka m’masunagoge a m’dziko lonse la Isiraeli, ngakhale kutali kwambili ku Makedoniya. (Luka 4:16, 17; Machitidwe 17:11) Kodi mipukutu yakale imeneyo inapulumuka bwanji?

1. Kapu ya dothi; 2. Mbali imodzi ya Mpukutu wa ku Nyanja Yakufa

Mipukutu ya ku Nyanja Yakufa inapezeka m’mitsuko imene anaisungila m’mapanga a m’zipululu. Mipukutuyi yakhalapo kwa zaka zambili

Phanga limene kunapezeka mipukutu ina ya Baibulo

Katswili wa Cipangano Catsopano dzina lake Philip W. Comfort anati: “Ayuda anali kukonda kuika mipukutu ya Malemba m’mitsuko kuti isungike bwino.” Mwacionekele, Akhiristu anapitiliza kucita zimenezo. Ndipo mipukutu ina yoyambilila ya Baibulo inapezeka m’mitsuko, m’zipinda zosungilamo zinthu, ndi m’mapanga. Ina anaipeza m’zipululu.

ZOTSATILAPO ZAKE: Mipukutu ya Baibulo masauzande ambili ikalipo. Ina mwa mipukutu imeneyo inalembedwa zaka zoposa 2,000 zapitazo. Palibe buku lina lakale limene lili ndi mipukutu yambili imene inalembedwa kale kwambili monga ya Baibulo.

a Gumbwa ndi zomela zinazake za m’madzi zimene kale anali kupangila mapepala.

b Mwacitsanzo, cikalata ca boma la United States coonetsa kuti dzikolo lalandila ufulu wodzilamulila cinalembedwa pa cikumba ca nyama. Koma tsopano n’cowonongeka kwambili cakuti mawu ambili anafutika ngakhale kuti papita zaka zosakwana 250.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani