LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 4/13 tsa. 7
  • Kubweleza za M’sukulu ya Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kubweleza za M’sukulu ya Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
km 4/13 tsa. 7

Kubweleza za M’sukulu ya Ulaliki

Tidzakambilana mafunso otsatilawa pa Sukulu ya Ulaliki mkati mwa mlungu wa April 29, 2013. Taonetsa deti la mlungu umene tidzaphunzila mfundo iliyonse. Tacita zimenezi kuti mlungu uliwonse tizitha kufufuza mfundozo pokonzekela.

1. Kodi ndi cikumbutso cofunika kwambili citi conena za cikwati cimene Yesu anapeleka pa Maliko 10:6-9? [Mar. 4, w08 2/15 tsa. 30 ndime 8]

2. Kodi kutumikila Yehova ndi mtima wonse kumatanthauza ciani? (Maliko 12:30) [Mar. 4, w97 10/15 tsa. 13 ndime 4]

3. Kodi “masautso” amene achulidwa pa Maliko 13:8 n’ciani? [Mar. 11, w08 3/15 tsa. 12 ndime 2]

4. Kodi ndi mabuku ati amene Luka anafufuzamo pamene anali kulemba Uthenga wake Wabwino? (Luka 1:3) [Mar. 18, w09 3/15 tsa. 32 ndime 4]

5. Kodi mfundo yakuti Satana amayesetsa kupeza nthawi yabwino yoti atiyese, iyenela kutilimbikitsa kucita ciani? (Luka 4:13) [Mar. 25, w11 1/15 tsa. 23 ndime 10]

6. Kodi mau opezeka pa Luka 6:27, 28, tingawagwilitsile nchito bwanji? [Mar. 25, w08 5/15 tsa. 8 ndime 4]

7. N’cifukwa ciani Yesu anakhululukila mai amene anali kudziŵika monga wocimwa iye asanamwalile monga nsembe ya dipo? (Luka 7:37, 48) [Apr. 1, w10 8/15 tsa. 6-7]

8. Kodi otsatila a Kristu afunika ‘kudana’ ndi acibale ao m’njila yotani? (Luka 14:26) [Apr. 15, w08 3/15 tsa. 32 ndime 1; w92 7/15 tsa. 9 ndime 3-5]

9. Kodi “zizindikilo padzuŵa, mwezi ndi nyenyezi” zidzakhudza motani anthu? (Luka 21:25) [Apr. 22, w97 4/1 tsa. 15 ndime 8-9]

10. Kodi tingatsanzile bwanji citsanzo ca Yesu ca kupemphela pamene tikumana ndi mavuto aakulu? (Luka 22:44) [Apr. 29, w07 8/1 tsa. 6 ndime 2]

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani