Ndandanda ya Mlungu wa May 27
MLUNGU WA MAY 27
Nyimbo 6 ndi Pemphelo
□ Phunzilo la Baibo la Mpingo:
bt Mutu 23 ndime 16-19 ndi bokosi patsamba 188 (Mph. 30)
□ Sukulu ya Ulaliki:
Kuŵelenga Baibo: Yohane 12-16 (Mph. 10)
Na. 1: Yohane 12:20-36 (Mph. 4 kapena zocepelapo)
Na. 2: Kodi Nsembe ya Yesu Inagwila Nchito Coyamba Kwa Ndani, Ndipo Colinga Cake Cinali Cotani?—rs tsa. 124 ndime 2-3 (Mph. 5)
Na. 3: N’cifukwa Ciani M’pomveka Kunena Kuti Yehova Ndi “Mulungu Amene Amapatsa Mtendele”?—Aroma 15:33 (Mph. 5)
□ Msonkhano wa Nchito:
Nyimbo 98
Mph. 5: Kuyambitsa Maphunzilo a Baibo pa Ciŵelu Coyamba. Nkhani. Onetsani mmene tingayambitsile phunzilo pa Ciŵelu coyamba mu June, mwa kugwilitsila nchito nkhani ili kucikuto cakumapeto kwa Nsanja ya Olonda. Limbikitsani onse kutengako mbali.
Mph. 15: Kuthilila Mbeu Zimene Tinabzala. (1 Akor. 3:6-9) Nkhani yokambilana yozikidwa pa mafunso otsatila: (1) N’ciani cimakusangalatsani popanga maulendo obwelelako? (2) Kodi n’ciani cimavuta ena kupanga maulendo obwelelako? (3) Kodi angalimbane nao bwanji mavuto amenewa? (4) Ndi kuti kumene tingapeze thandizo ngati zimativuta kupanga maulendo obwelelako? (5) Kodi mumacita ciani kuti mukumbukile munthu amene anasonyeza cidwi ndi kuti mukumbukile nkhani imene munakambilana naye, cofalitsa cimene munam’siila, ndi zinthu zina zokhudza munthuyo? (6) Kodi mumakonzekela bwanji maulendo anu obwelelako? (7) N’cifukwa ciani ndi bwino kukhala ndi ndandanda mlungu uliwonse ya maulendo obwelelako?
Mph. 10: “Pemphani Zimene Mufuna.” Kukambilana. Funsani omvela kuti afotokoze mmene apindulila mwa kugwilitsila nchito zofalitsa zimene zinatulutsidwa posacedwapa m’cinenelo cao.
Nyimbo 101 ndi Pemphelo