Ndandanda ya Mlungu wa September 2
MLUNGU WA SEPTEMBER 2
Nyimbo 47 ndi Pemphelo
□ Phunzilo la Baibo la Mpingo:
bt mutu 28 ndime 8 mpaka 15 (Mph. 30)
□ Sukulu ya Ulaliki:
Kuŵelenga Baibo: 1 Akorinto 1 mpaka 9 (Mph. 10)
Na. 1: 1 Akorinto 4:18–5:13 (Mph. 4 kapena zocepelapo)
Na. 2: Kodi Munthu Akamaona Kuti Akudziŵa Kwambili Anthu Kapena Malo Ena Ake Atsopano, Kodi Ndi Umboni Wakuti Munthu Akafa Amakabadwanso Kwinakwake?—rs tsa. 174 ndime 3-tsa. 176 ndime 1 (Mph. 5)
Na. 3: Kodi Mkristu Angatani Kuti Akhalebe Wosangalala Ngakhale Kuti Akudwala?—Afil. 4: 6, 7 (Mph. 5)
□ Msonkhano wa Nchito:
Nyimbo 72
Mph. 10: Zimene Mungakambe Pogaŵila Magazini mu September. Kukambilana. Fotokozani cifukwa cake magazini awa adzakhala okopa anthu a m’gawo lanu. Citani zimenezi kwa tumphindi 30 mpaka 60. Ndiyeno, pa nkhani zoyambilila zogwilizana ndi mutu wa pacikuto ca Nsanja ya Mlonda, pemphani omvela kuti achule funso lodzutsa cidwi limene angafunse poyambitsa makambilano, ndi lemba limene angaŵelenge. Citani cimodzi-modzi ndi Galamukani! komanso ngati nthawi ilola, citaninso cimodzi-modzi ndi nkhani ina imodzi ya mu Nsanja ya Mlonda kapena Galamukani! Citani citsanzo ca mmene mungagaŵilile magazini iliyonse.
Mph. 10: Zosoŵa za pampingo.
Mph. 10: Tsatilani Citsanzo ca Baranaba. Nkhani yokambilana. Pemphani omvela kuti anene mmene kutsatila citsanzo ca Baranaba kungawathandizile monga alaliki.
Nyimbo 65 ndi Pemphelo