LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 8/14 tsa. 1
  • Ndandanda ya Mlungu wa August 11

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Ndandanda ya Mlungu wa August 11
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Tumitu
  • MLUNGU WA AUGUST 11
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 8/14 tsa. 1

Ndandanda ya Mlungu wa August 11

MLUNGU WA AUGUST 11

Nyimbo 71 ndi Pemphelo

Phunzilo la Baibulo la Mpingo:

jr mutu 12 ndime 8 mpaka 13 (Mph. 30)

Sukulu ya Ulaliki:

Kuŵelenga Baibulo: Numeri 7-9 (Mph. 10)

Na. 1: Numeri 9:9-23 (Mph. 4 kapena zocepelapo)

Na. 2: Munthu Akapulumutsidwa Sizitanthauza kuti Wapulumutsidwa Nthawi Yonse—rs tsa. 96 ndime 3-6 (Mph. 5)

Na. 3: Kodi Tiziopa Anthu Akufa?—bh tsa.58 ndime 5-6  (Mph. 5)

Msonkhano wa Nchito:

Nyimbo 107

Mph. 5: “1914-2014: Ufumu Wakhala Ukulamulila Kwa Zaka 100!” Nkhani yokambilana. Ŵelengani ndime imene ili pamwamba pa tsamba lino. Mbali za Msonkhano wa Nchito mwezi uno zidzafotokoza kwambili za Ufumu. Fotokozani makonzedwe a mpingo wanu a ulaliki wakumunda.

Mph. 10: “Gwilitsilani Nchito Kapepala Katsopano Konena za Webusaiti Yathu.” Kambilanani zimene zili m’kapepala kameneka. Ndiyeno citani citsanzo coonetsa wofalitsa akugaŵila kapepala kameneka ndiyeno akuonetsa munthuyo kapepala pa jw.org pogwilitsila nchito foni yake yokhala ndi Intaneti kapena kacida kena kake.

Mph. 15: “Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Kulankhula za Ufumu Molimba Mtima.” Nkhani yokambilana. Ofalitsa aŵili acite citsanzo pa zocitika izi: Wofalitsa ali pa mzele m’sitolo. Ndiyeno munthu wina kumbuyo kwake akuŵelenga nyuzipepala ndipo akunena kuti: “Koma zinthu zaipilatu m’dzikoli! Anthu onse amaganiza kuti ali ndi yankho koma zinthu zingoipilaipilabe.” Tsopano wofalitsa akudzilankhulila yekha kuti ‘sindifunika kukhala cete. Ndifunika ndilankhule za Ufumu basi!’ Wofalitsa akuti: “N’zoona zinthu zaipa kwambili. Koma kodi mungakonde kulandila kapepala aka? Kakufotokoza za Webusaiti imene yandithandiza kupeza mayankho pa mafunso ofunika kwambili.” Wofalitsa afotokoze mfundo imodzi ya m’kapepalako, ndipo munthuyo aonetse kuti wacita cidwi.

Nyimbo 92 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani