LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 8/14 tsa. 3
  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 8/14 tsa. 3

Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Tidzakambilana mafunso otsatilawa pa Sukulu ya Ulaliki mkati mwa mlungu wa August 25, 2014.

  1. Kodi lemba la Levitiko 18:3 lingatithandize bwanji kupewa kukhala ndi maganizo olakwika a cabwino ndi coipa? (Aef. 4:17-19) [July 7, w02 2/1 tsa. 29 ndime 4]

  2. Tiphunzilapo ciani pa lamulo lopezeka pa Levitiko 19:2? Nanga n’cifukwa ciani tiyenela kuyesetsa kulimvela? [July 7, w09 7/1 tsa. 9 ndime 5]

  3. Kodi lamulo lakale lokhudza kukunkha limatiphunzitsa ciani? (Lev. 19:9, 10) [July 7, w06 6/15 mas. 22-23 ndime 13]

  4. N’cifukwa ciani tinganene kuti lamulo lakuti “diso kulipila diso” silinali kulimbikitsa mfundo yobwezela? (Lev. 24:19, 20) [July 14, w09 9/1 tsa. 22 ndime 3-4]

  5. Ndi liti pamene kunali kulakwa kwa Mwiisiraeli kupempha ciongoladzanja pa ndalama zimene wabweleketsa wina? Nanga ndi liti pamene kunali kololeka kupempha ciongoladzanja? (Lev. 25:35-37) [July 21, w04 5/15 tsa. 24 ndime 3]

  6. N’cifukwa ciani nthawi zambili Baibulo limangochula mafuko 12 a Isiraeli koma kwenikweni anali mafuko 13? (Num. 1:49, 50) [July 28, w08 7/1 tsa. 21]

  7. Ndi phunzilo lotani lonena za kuganizila okalamba limene tiphunzilapo pa lemba la Numeri 8:25, 26 ponena za nchito yokakamiza? [Aug. 11, w04 8/1 tsa. 25 ndime 1]

  8. Atatuluka mu Iguputo mozizwitsa, n’cifukwa ciani Aisiraeli anayamba kudandaula? Nanga ndi phunzilo lofunika liti limene tikuphunzila pankhani imeneyi? (Num. 11:4-6) [Aug. 18, w95 3/1 tsa. 15-16 ndime 10]

  9. Tiphunzilapo ciani pa zimene Mose anacita Elidadi ndi Medadi atakhala aneneli? (Num. 11:27-29) [Aug. 18, w04 8/1 tsa. 26 ndime 4]

  10. Ndi phunzilo lofunika liti limene tiphunzilapo pa lamulo limene linapatsidwa kwa Aisiraeli lakuti “azisokelela mphonje m’mphepete mwa zovala zao”? (Num. 15:37-39) [Aug. 25, w04 8/1 tsa. 26 ndime 7]

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani