Ndandanda ya Mlungu wa November 17
MLUNGU WA NOVEMBER 17
Nyimbo 132 ndi Pemphelo
Phunzilo la Baibulo la Mpingo:
cl mutu 1 ndime 1 mpaka 9, ndi bokosi patsamba 3 (Mph. 30)
Sukulu ya Ulaliki:
Kuŵelenga Baibulo: Deuteronomo 23-27 (Mph. 10)
Na. 1: Deuteronomo 25:17–26:10 (Mph. 4 kapena zocepelapo)
Na. 2: Zimene Baibulo Limanena pa Nkhani ya Moyo—rs tsa. 295 ndime 1–5 (Mph. 5)
Na. 3: Njila Yokhayo Yoyenela Kugwilitsila Nchito Magazi—bh tsa 131-133 ndime 17-19 (Mph. 5)
Msonkhano wa Nchito:
Nyimbo 118
Mph. 10: Bwenzi Lenileni Ndani? Kukambilana kozikidwa pa tukadoli twa pa Webusaiti yathu pa mutu wakuti What’s a Real Friend? (Pitani pa jw.org, ndi kuona polemba kuti BIBLE TEACHINGS > TEENAGERS.) Yambani ndi kuonelela vidiyo pamodzi ndi omvela. Ngati zimenezi n’zosatheka, kambitsilanani mfundo zimene zili m’bokosi lopezeka patsamba 29 ndi 30, m’buku lakuti Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu. Kenako kambilanani pogwilitsila nchito mafunso awa: (1) Kodi bwenzi lenileni ndi munthu wotani? (2) Ndi zinthu ziti zimene mungaone mwa munthu amene mufuna kuti akhale bwenzi lanu? (3) Mungapeze bwanji bwenzi labwino? (4) Ndi zinthu ziti zimene mufunika kucita kuti mulimbitse ubwenzi wanu?
Mph. 10: Timadziŵika Cifukwa ca Cikondi. (Yohane 13:35) Kukambilana kocokela mu Buku la pacaka la 2014, tsamba 48, ndime 1, mpaka tsamba 49, ndime 3, ndi tsamba 69, ndime 1, mpaka tsamba 70, ndime 2. Pemphani omvela kuti anene zimene aphunzilapo.
Mph. 10: “Njila ina Yokondweletsa Ndiponso Yatsopano Yocitila Ulaliki Wapoyela.” Mafunso ndi mayankho. Ngati mpingo uli ndi malo amene pamapita anthu ambili, funsani woyang’anila nchito kuti afotokoze zimene mpingo wakonza ponena za ulaliki wapoyela. Ndiyeno pemphani omvela kuti asimbe zocitika za mu ulaliki umenewu.
Nyimbo 92 ndi Pemphelo