LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 5/15 tsa. 4
  • Zocitika Zokhudza Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Zocitika Zokhudza Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
km 5/15 tsa. 4

Zocitika Zokhudza Ulaliki

Tili ndi zifukwa zambili zokhalila okondwela tikaona lipoti la caka cautumiki ca 2014. Anthu oposa 790,000 anapezeka pa Cikumbutso. Tinali ndi ciwelengelo capamwamba ca ofalitsa okwanila 170,245. Ofalitsa okwanila 28,737 anacita upainiya wokhazikika komanso wothandiza m’mwezi wina. Cosangalatsanso kwambili n’cakuti anthu pafupifupi 1,000 anabwezeletsedwa mumpingo. (Luka 15:32) Ulaliki wa m’mizinda ikuluikulu wakhala ukukopa anthu ambili mwezi ulionse. Pa avaleji zofalitsa zoposa 7,000, zimagaŵilidwa mwezi uliwonse pa malo okwanila 5 mu Lusaka ndipo abale amapanga maulendo obwelelako kwa anthu acidwi ambilimbili kaamba ka ulaliki umenewu. Tikuthokoza kwambili Yehova kaamba kotithandiza ndipo tikuyamikila inu nonse amene mwa cikhulupililo munalengeza “uthenga wabwino waulemelelo.”—2 Akor. 4:4.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani