UMOYO WATHU WACIKHRISTU
Pangitsani Phunzilo Lanu Laumwini Kukhala Lopindulitsa
CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Phunzilo laumwini limatithandiza ‘kudziŵa bwino m’lifupi, m’litali, kukwela, na kuzama’ kwa coonadi. (Aef. 3:18) Limatithandizanso kuti tikhale opanda cifukwa cotineneza naco, osalakwa m’dziko lino loipa komanso “kugwila mwamphamvu mawu amoyo.” (Afil. 2:15, 16) Pa phunzilo laumwini timasankha nkhani zimene tifuna kuphunzila. Tingacite ciani kuti tizipindula mofikapo pamene tiŵelenga na kuphunzila Baibo?
MMENE TINGACITILE:
Congani mavesi na kulemba mfundo m’Baibo yanu yopulinta kapena ya pa cipangizo
Poŵelenga Mawu a Mulungu, dzifunseni mafunso aya: ‘N’ndani? N’ciani? Liti? N’kuti? Cifukwa ciani? Motani?’
Pezani mfundo. Seŵenzetsani zida zofufuzila zimene zilipo. Mungafufuze mwa kuseŵenzetsa mutu wa nkhani kapena lemba
Muzisinkha-sinkha zimene mwaŵelenga kuti muone mmene mfundozo zingakuthandizileni mu umoyo wanu
Seŵenzetsani zimene mwaphunzila mu umoyo wanu.—Luka 6:47, 48
TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI PITILIZANI “KUGWILA MWAMPHAMVU” MWA KUCITA PHUNZILO LAUMWINI LOPINDULITSA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:
Kodi ena amacita bwanji phunzilo laumwini?
N’cifukwa ciani tifunika kupemphela tisanayambe phunzilo laumwini?
N’ciani cingatithandize kuimvetsa bwino Baibo?
Ni zizindikilo zanji zimene tingaike m’Baibo imene timaseŵenzetsa?
N’cifukwa ciani kusinkha-sinkha n’kofunika poŵelenga Mawu a Mulungu?
Kodi tiyenela kucita nazo ciani zimene timaŵelenga?
“Ndimakonda kwambili cilamulo canu! Ndimasinkha-sinkha cilamuloco tsiku lonse.”—Sal. 119:97