LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 June tsa. 8
  • Pangitsani Phunzilo Lanu Laumwini Kukhala Lopindulitsa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Pangitsani Phunzilo Lanu Laumwini Kukhala Lopindulitsa
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Khalani na Cizoloŵezi Cabwino Coŵelenga
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
  • N’ciyani Cingakuthandizeni Kuti Musaleke Kuphunzila Baibo?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 June tsa. 8

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Pangitsani Phunzilo Lanu Laumwini Kukhala Lopindulitsa

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Phunzilo laumwini limatithandiza ‘kudziŵa bwino m’lifupi, m’litali, kukwela, na kuzama’ kwa coonadi. (Aef. 3:18) Limatithandizanso kuti tikhale opanda cifukwa cotineneza naco, osalakwa m’dziko lino loipa komanso “kugwila mwamphamvu mawu amoyo.” (Afil. 2:15, 16) Pa phunzilo laumwini timasankha nkhani zimene tifuna kuphunzila. Tingacite ciani kuti tizipindula mofikapo pamene tiŵelenga na kuphunzila Baibo?

MMENE TINGACITILE:

  • Congani mavesi na kulemba mfundo m’Baibo yanu yopulinta kapena ya pa cipangizo

  • Poŵelenga Mawu a Mulungu, dzifunseni mafunso aya: ‘N’ndani? N’ciani? Liti? N’kuti? Cifukwa ciani? Motani?’

  • Pezani mfundo. Seŵenzetsani zida zofufuzila zimene zilipo. Mungafufuze mwa kuseŵenzetsa mutu wa nkhani kapena lemba

  • Muzisinkha-sinkha zimene mwaŵelenga kuti muone mmene mfundozo zingakuthandizileni mu umoyo wanu

  • Seŵenzetsani zimene mwaphunzila mu umoyo wanu.—Luka 6:47, 48

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI PITILIZANI “KUGWILA MWAMPHAMVU” MWA KUCITA PHUNZILO LAUMWINI LOPINDULITSA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • Kodi ena amacita bwanji phunzilo laumwini?

  • N’cifukwa ciani tifunika kupemphela tisanayambe phunzilo laumwini?

  • N’ciani cingatithandize kuimvetsa bwino Baibo?

  • Ni zizindikilo zanji zimene tingaike m’Baibo imene timaseŵenzetsa?

  • N’cifukwa ciani kusinkha-sinkha n’kofunika poŵelenga Mawu a Mulungu?

  • Kodi tiyenela kucita nazo ciani zimene timaŵelenga?

Mlongo akucita phunzilo la Baibo laumwini mozama; m’bale akuconga Baibo yake na mitundu yosiyana-siyana; mlongo akuŵengela amuna aŵili manotsi amene analemba m’Baibo yake; m’bale akupemphela

“Ndimakonda kwambili cilamulo canu! Ndimasinkha-sinkha cilamuloco tsiku lonse.”—Sal. 119:97

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani