LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 February tsa. 5
  • Mmene Mwamuna na Mkazi Wake Angalimbitsile Cikwati Cawo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mmene Mwamuna na Mkazi Wake Angalimbitsile Cikwati Cawo
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Tetezani Cikwati Canu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Pambuyo Pa Tsiku La Cikwati
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Cikwati Ni Mphatso Yocokela Kwa Mulungu
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Cikwati Ndi Mphatso Yocokela kwa Mulungu Wacikondi
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 February tsa. 5
Abulamu na Sarai akukonzekela kucoka mu mzinda wa Uri. Abulamu wanyamula thumba lalikulu lonyamulilamo zinthu, ndipo akulimbikitsa Sarai amene akuika zinthu m’basiketi.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Mmene Mwamuna na Mkazi Wake Angalimbitsile Cikwati Cawo

Abulahamu na Sara anali citsanzo cabwino monga mwamuna na mkazi wake amene anali kukondana na kulemekezana. (Gen. 12:11-13; 1 Pet. 3:6) Ngakhale n’conco, cikwati cawo sicinali cangwilo, anafunika kupilila mayeselo mu umoyo wawo. Kodi okwatilana angaphunzile ciani pa citsanzo ca Abulahamu na Sara?

Muzikambilana. Yankhani modekha ngati mnzanu wa m’cikwati akukamba motaya mtima kapena mokhumudwa. (Gen. 16:5, 6) Muzipatula nthawi yocezela pamodzi. Mwa mawu na zocita zanu, onetsani mnzanuyo kuti mumam’konda. Koposa zonse, ikani Yehova patsogolo m’cikwati canu. Citani izi mwa kuŵelengela pamodzi, kupemphela, komanso kulambilila pamodzi. (Mlaliki 4:12) Zikwati zolimba zimalemekeza Yehova, amene anakhazikitsa makonzedwe opatulika amenewa.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI ZIMENE MUNGACITE KUTI MULIMBITSE CIKWATI CANU, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • Mu vidiyoyi, mwaona zizindikilo zotani zoonetsa kuti Shaan na Kiara anayamba kutalikilana?

  • N’cifukwa ciani kukambilana momasuka komanso moona mtima n’kofunika m’cikwati?

  • Kodi citsanzo ca Abulahamu na Sara cinathandiza bwanji Shaan na Kiara?

  • Kodi Shaan na Kiara anatenga masitepu ati kuti alimbitse cikwati cawo?

  • N’cifukwa ciani mwamuna na mkazi wake sayenela kuyembekezela ungwilo m’cikwati cawo?

Zithunzi: Zocitika za m’vidiyo yakuti ‘Zimene Mungacite Kuti Mulimbitse Cikwati Canu.’ Shaan na Kiara atenga masitepu oyenelela kuti alimbitse cikwati cawo. 1. Iwo akhala cake-cake pampando umodzi. 2. Iwo agwilana manja. 3. Akuseŵenza pamodzi mosangalala mu ulaliki.

N’zotheka ndithu kulimbitsa cikwati canu!

Kuti mumve zambili za mmene mungalimbitsile cikwati canu, ŵelengani nkhani zotsatilazi zimene zinatuluka mu Galamukani! komanso pa jw.org®:

  • “Ana Akakula N’kucoka Pakhomo”—g17.4 10-11

  • “Mungatani Kuti Musamakangane Pokambilana Mavuto Anu?”—g16.3 10-11

  • “Ngati Banja Lanu Silikuyenda Bwino”—g 3/14 14-15

  • “Kodi Mungatani Kuti Muzimvetsela Mwamuna Kapena Mkazi Wanu Akamalankhula?” —g 12/13 12-13

  • “Zimene Mungacite Kuti Musamakangane” —g 2/13 4-5

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani