LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 October tsa. 5
  • Acinyamata—Kodi Yehova ni Bwenzi Lanu Lapamtima?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Acinyamata—Kodi Yehova ni Bwenzi Lanu Lapamtima?
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Mukhoza Kukhala Bwenzi la Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mulungu Akupemphani Kuti Mukhale Mnzake
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Yehova Ndi Bwenzi Lathu Lapamtima
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Kukhala Bwenzi la Yehova
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 October tsa. 5
M’bale wacicepele wakhala ku thebulo ndipo maganizo ake onse ali pa kucita phunzilo laumwini.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Acinyamata—Kodi Yehova ni Bwenzi Lanu Lapamtima?

Kodi ni munthu wa makhalidwe otani amene mumafuna atakhala mnzanu? Mwacionekele mumafuna atakhala wokhulupilika, wokoma mtima, komanso wowoloŵa manja. Yehova ali nawo makhalidwe onse amenewa. (Eks. 34:6; Mac. 14:17) Mulungu amamvetsela mukamapemphela kwa iye. Amakuthandizani mukafunika thandizo. (Sal. 18:19, 35) Amakukhululukilani mukalakwa. (1 Yoh. 1:9) Ndithudi, Yehova ni Bwenzi labwino ngako!

Kodi mungacite ciani kuti mukhale bwenzi la Yehova? Phunzilani za iye mwa kuŵelenga Mawu ake. Muuzeni za mumtima mwanu komanso nkhawa zanu. (Sal. 62:8; 142:2) Onetsani kuti mumakonda zinthu zimene Yehova amaona kuti n’zofunika. Zinthu monga Mwana wake, Ufumu wake, komanso malonjezo ake. Muziuzako ena za Mulungu. (Deut. 32:3) Mukapanga ubwenzi wolimba na Yehova, iye adzakhala Bwenzi lanu kwamuyaya.—Sal. 73:25, 26, 28.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI ACINYAMATA—“TALAWANI NDIPO MUONE KUTI YEHOVA NDI WABWINO,” NDIPO PAMBUYO PAKE YANKHANI MAFUNSO AWA:

  • Zocitika za mu vidiyo yakuti ‘Acinyamata—Talawani Ndipo Muone Kuti Yehova Ndi Wabwino.’ Mlongo wacicepele akupemphela asanayambe kucita phunzilo laumwini.

    Mungakonzekele bwanji kudzipatulila kwa Mulungu na ubatizo?

  • Zocitika za mu vidiyo yakuti ‘Acinyamata—Talawani Ndipo Muone Kuti Yehova Ndi Wabwino.’ M’bale amene ni mpainiya akuŵelengela lemba mwamuna wina m’citundu ca ci Karen (S’gaw).

    Kodi ena mumpingo angakuthandizeni bwanji kutumikila Yehova?

  • Zocitika za mu vidiyo yakuti ‘Acinyamata—Talawani Ndipo Muone Kuti Yehova Ndi Wabwino.’ M’bale wacicepele amene amayamikila thandizo la acikulile, akupitila pamodzi mu ulaliki na wacikulile.

    Kodi kulalikila kungalimbitse bwanji ubale wanu na Yehova?

  • Zocitika za mu vidiyo yakuti ‘Acinyamata—Talawani Ndipo Muone Kuti Yehova Ndi Wabwino.’ Mlongo amene wayenda wapansi kwa maawazi aŵili, akutsogoza phunzilo mtsikana wogontha.

    Mungathe kukhala pa ubwenzi na Yehova kwamuyaya!

    Ni mautumiki ati m’gulu la Mulungu amene mungaciteko?

  • N’ciani cimene mumakonda kwambili ponena za Yehova?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani