LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb24 July masa. 14-15
  • August 26–September 1

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • August 26–September 1
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2024
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2024
mwb24 July masa. 14-15

AUGUST 26–SEPTEMBER 1

MASALIMO 78

Nyimbo 97 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Zithunzi: Mwiisiraeli akukumbukila umoyo wakale wa ku Iguputo pamene akuuluza mana na dzanja lake. 1. Iye anali kudya vwembe. 2. Aiguputo anali kumenya Aisiraeli amene anali akapolo na kuwacitila nkhanza.

1. Citsanzo Coticenjeza ca Aisiraeli Osakhulupilika

(Mph. 10)

Aisiraeli anaiŵala nchito zodabwitsa za Yehova (Sal. 78:​11, 42; w96-CN 12/1 29-30)

Aisiraeli sanayamikile zimene Yehova anawapatsa (Sal. 78:19; w06-CN 7/15 17 ¶16)

Aisiraeli sanaphunzilepo kanthu pa zolakwa zawo. M’malo mwake, anali kukhala osakhulupilika nthawi zambili (Sal. 78:​40, 41, 56, 57; w11-CIN 7/1 10 ¶3-4)


ZOFUNIKA KUZISINKHASINKHA: N’ciyani cingatithandize kupewa kukhala osakhulupilika kwa Yehova?

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Sal. 78:​24, 25—N’cifukwa ciyani mana amachedwa “tiligu wocokela kumwamba” ndiponso “cakudya ca amphamvu”? (w06-CN 7/15 11 ¶5)

  • Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo ziti zothandiza zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuŵelenga Baibo

(Mph. 4) Sal. 78:​1-22 (th phunzilo 5)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NA NYUMBA. Yambitsani phunzilo la Baibo. (lmd phunzilo 5 mfundo 5)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NA NYUMBA. Seŵenzetsani kathilakiti poyambitsa makambilano. Yambitsani phunzilo la Baibo. (lmd phunzilo 5 mfundo 4)

6. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 1) KUNYUMBA NA NYUMBA. Mwini nyumba wakuuzani kuti mukambe mwacidule. Yambitsani phunzilo la Baibo. (lmd phunzilo 2 mfundo 5)

7. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) ULALIKI WAMWAYI. Popanda kukamba coonadi ca m’Baibo, pezani njila imene ingathandize munthu amene mukukamba naye kudziŵa kuti ndinu wa Mboni za Yehova, kenako yambitsani phunzilo. (lmd phunzilo 2 mfundo 4)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 96

8. Phunzilani pa Citsanzo ca Mlaliki Filipo

(Mph. 15) Kukambilana.

Mlaliki Filipo akufotokozela Malemba mwamuna wa ku Itiyopiya amene ali mu galeta lake.

M’Malemba muli zitsanzo zambili zabwino na zoipa. Kuti titengepo phunzilo pa zitsanzo zimenezi, tiyenela kupatula nthawi komanso kucita khama. Kuwonjezela pa kuŵelenga nkhani za m’Baibo, tiziganizila zimene tiphunzilapo na kupanga masinthidwe ofunikila.

Mlaliki Filipo anali Mkhristu wodziŵika kuti anali na “mzimu komanso nzelu.” (Mac. 6:​3, 5) Kodi tiphunzilapo ciyani pa citsanzo cake?

Tambitsani VIDIYO yakuti Zimene Tingaphunzile kwa Iwo—Mlaliki Filipo. Ndiyeno funsani omvetsela zimene aphunzilapo pa mbali zotsatila izi:

  • Zimene Filipo anacita zinthu zitasintha mwadzidzidzi.—Mac. 8:​1, 4, 5

  • Madalitso amene Filipo anapeza cifukwa cokhala wokonzeka kupita kumene kunali kufunikila anchito ambili.—Mac. 8:​6-8, 26-31, 34-40

  • Mapindu amene Filipo na banja lake anapeza cifukwa cokhala woceleza.—Mac. 21:​8-10

  • Cimwemwe cimene banja la muvidiyo iyi linapeza kaamba kotsatila citsanzo ca Filipo

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) bt mutu 14 ¶11-20

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 101 na Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani