LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb24 September masa. 10-11
  • October 7-13

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • October 7-13
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2024
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2024
mwb24 September masa. 10-11

OCTOBER 7-13

MASALIMO 92-95

Nyimbo 84 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kutumikila Yehova Ndiwo Umoyo Wabwino Koposa!

(Mph. 10)

Yehova ni woyenela kulambilidwa (Sal. 92:1, 4; w18.04 26 ¶5)

Iye amapatsa anthu ake luso la kuzindikila (Sal. 92:5; w18.11 20 ¶8)

Iye amakonda anthu amene amamutumikila ngakhale mu ukalamba wawo (Sal. 92:12-15; w20.01 19 ¶18)

Zithunzi: 1. Mzimayi wacitsikana akupemphela. 2. Iye akubatizika.

DZIFUNSENI KUTI, ‘N’ciyani cikunilepheletsa kudzipatulila kwa Yehova na kubatizika?’

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Sal 92:5​—N’cifukwa ciyani tinganene kuti mawu awa afotokoza bwino nzelu za Yehova? (cl-CN 176 ¶18)

  • Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuŵelenga Baibo

(Mph. 4) Sal. 94:1-23 (th phunzilo 5)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) ULALIKI WAMWAYI. Pokambilana na munthu pezani njila yomuthandizila kudziŵa zimene mumacita monga mphunzitsi wa Baibo. (lmd phunzilo 5 mfundo 3)

5. Kubwelelako

(Mph. 3) ULALIKI WAMWAYI. Yambitsani phunzilo la Baibo kwa munthu amene pa nthawi ina anakana kuphunzila. (lmd phunzilo 8 mfundo 4)

6. Kupanga Ophunzila

(Mph. 5) Kambilanani na wophunzila amene sakupita patsogolo. (lmd phunzilo 12 mfundo 5)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 5

7. Acicepele Akakhala na Nkhawa Yaikulu

(Mph. 15) Kukambilana.

Mtsikana amene watiyilatu ciyembekezo akuyang’ana pansi.

Ifenso atumiki a Yehova timakhala na nkhawa. Mwacitsanzo, Davide anali kukhala na nkhawa nthawi zina, ndipo ni mmenenso zilili kwa abale athu ambili masiku ano. (Sal. 13:2; 139:23) N’zacisoni kuti ngakhale acicepele amavutika na nkhawa. Nthawi zina, nkhawa ingacititse wacicepele kuona zinthu zimene amacita nthawi zonse kukhala zovuta, monga kupita kusukulu kapena kupezeka ku misonkhano ya mpingo. Nthawi zinanso, ingamupangitse kukhala na mantha aakulu kapena maganizo ofuna kudzipha.

Acicepele, mukapanikizika cifukwa ca nkhawa, uzan’koni makolo anu kapena munthu wina wokhwima maganizo. Musaiŵalenso kupempha Yehova kuti akuthandizeni. (Afil. 4:6) Iye adzakuthandizani. (Sal. 94:17-19; Yes 41:10) Ganizilani citsanzo ca m’bale Steing.

Tambitsani VIDIYO YAKUTI Yehova Amanikonda. Kenako funsani omvela kuti:

• Ni lemba liti linathandiza m’bale Steing? Nanga n’cifukwa ciyani?

• Kodi Yehova anamuthandiza bwanji?

Mtsikana wa pa cithunzi capita akufotokozela makolo ake momasuka mmene akumvela. Iwo akumvetsela mwachelu.

Inu makolo, thandizani ana anu kucepetsa nkhawa mwa kuŵamvetsela moleza mtima, kuŵaonetsa cikondi, komanso kuŵathandiza kukhulupilila kuti Yehova amaŵakondadi. (Tito 2:4; Yak. 1:19) Dalilani Yehova kuti akupatseni mphamvu n’colinga coti muzitha kulimbikitsa ana anu.

Nthawi zina sitingadziŵe kuti wina wake mu mpingo ali na nkhawa yaikulu, kapena sitingamvetse mmene akumvela. Ngakhale n’telo, tingathandizebe mwa kuonetsa cikondi kwa onse mu mpingo komanso kuwaona kuti ni ofunika.​—Miy. 12:25; Aheb. 10:24.

8. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) bt mutu 16 ¶6-9, bokosi pa tsa. 132

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 81 na Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani