LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 July masa. 14-15
  • August 25-31

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • August 25-31
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 July masa. 14-15

AUGUST 25-31

MIYAMBO 28

Nyimbo 150 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba(Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kusiyana Pakati pa Munthu Woipa ndi Munthu Wolungama

(Mph. 10)

Munthu woipa ndi wamantha koma wolungama amakhala wolimba mtima (Miy. 28:1; w93-CN 5/15 26 ¶2)

Munthu woipa sangapange zisankho zanzelu koma wolungama amatha kupanga zisankho zanzelu (Miy. 28:5; it-2-E 1139 ¶3)

Munthu wolungama amene ndi wosauka ali bwino kuposa munthu woipa amene ndi wolemela (Miy. 28:6; it-1-E 1211 ¶4)

M’bale wakhala pansi m’ndende ndipo mopanda mantha akupemphela atayang’ana m’mwamba.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 28:14​—Kodi mwambi uwu ukuticenjeza za ciyani? (w01-CN 12/1 11 ¶3)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Miy. 28:​1-17 (th phunzilo 10)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambilanani mmene nkhondo ndi ciwawa zidzathele. (lmd phunzilo 5 mfundo 5)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambilanani mmene nkhondo ndi ciwawa zidzathele. (lmd phunzilo 5 mfundo 4)

6. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 2) ULALIKI WAPOYELA. Kambilanani mmene nkhondo ndi ciwawa zidzathele. (lmd phunzilo 1 mfundo 4)

7. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) ULALIKI WAMWAYI. Kambilanani mmene nkhondo ndi ciwawa zidzathele. (lmd phunzilo 2 mfundo 4)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 112

8. Kodi Mumadana ndi Ciwawa?

(Mph. 6) Kukambilana.

Mnyamata watengeka ndi gemu imene akuchaya.

Amene anayambitsa ciwawa ndi Satana Mdyelekezi, mdani wamkulu wa Mulungu, yemwe Yesu anamuchula kuti “wakupha.” (Yoh. 8:44) Angelo ena atagwilizana ndi Satana n’kupandukila Mulungu, dziko lapansi linadzadza ndi ciwawa moti Mulungu anaona kuti linali litaipa. (Gen. 6:11) Masiku anonso dzikoli ladzala ndi ciwawa. Pamene mapeto akuyandikila, anthu oopsa komanso osadziletsa akuculukilaculukila.​—2 Tim. 3:​1, 3.

Welengani Salimo 11:5. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi Yehova amawaona bwanji anthu aciwawa, ndipo n’cifukwa ciyani?

  • Kodi masewela komanso zosangalatsa za masiku ano zimaonetsa bwanji kuti anthu amakonda zaciwawa?

Welengani Miyambo 22:​24, 25. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi zosangalatsa zimene timasankha komanso anthu amene timaceza nawo zingakhudze bwanji mmene timaonela zaciwawa?

  • Kodi zosangalatsa zimene timasankha zingaonetse bwanji kuti timakonda zaciwawa?

9. Kampeni Yapadela mu September

(Mph. 9)

Nkhani yokambidwa ndi woyang’anila utumiki. Limbikitsani ofalitsa kutengako mbali mokwanila pa kampeniyi, ndipo fotokozani zimene mpingo wakonza.

Tambitsani VIDIYO yakuti Mtendele Wosatha Pamapeto Pake! (Nyimbo ya Pamsonkhano Wacigawo wa 2022)

10. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 2 ¶19-27

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 50 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani