LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 July masa. 12-13
  • August 18-24

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • August 18-24
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 July masa. 12-13

AUGUST 18-24

MIYAMBO 27

Nyimbo 102 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Mmene Timapindulila Tikakhala ndi Mabwenzi Enieni

(Mph. 10)

Mabwenzi enieni amalimba mtima kutipatsa uphungu wofunikila (Miy. 27:​5, 6; w19.09 5 ¶12)

Mabwenzi enieni angathe kutithandiza bwino kwambili kuposa acibale athu (Miy. 27:10; it-2-E 491 ¶3)

Mabwenzi enieni amatithandiza kukhala anthu abwino (Miy. 27:17; w23.09 10 ¶7)

M’bale wacinyamata akuthandiza m’bale wacikulile kukambilana ndi dokotala.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 27:21​—Kodi zimene timacita tikatamandidwa zimaonetsa bwanji mmene umunthu wathu ulili? (w06-CN 9/15 19 ¶12)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Miy. 27:​1-17 (th phunzilo 5)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Munthuyo si wacipembedzo ca Cikhristu. (lmd phunzilo 6 mfundo 5)

5. Kubwelelako

(Mph. 4) ULALIKI WAMWAYI. Gwilitsani nchito vidiyo ya m’thuboksi yathu. (lmd phunzilo 8 mfundo 3)

6. Nkhani

(Mph. 5) ijwyp nkhani 75​—Mutu: Ndingatani Ngati Mnzanga Atandikhumudwitsa? (th phunzilo 14)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 109

7. “M’bale Amene Anabadwa Kuti Akuthandize Pakagwa Mavuto”

(Mph. 15) Kukambilana.

Yehova watipatsa gulu la abale la padziko lonse mmene tingapezemo mabwenzi acikondi. Ngakhale kuti tingakhale ndi mabwenzi ambili mumpingo, kodi ndi angati omwe ndi mabwenzi athu apamtima? Ubwenzi umalimba ngati pali kumvetsetsana, kudalilana, kukambilana mocokela pansi pamtima, kucitila zinthu pamodzi, komanso ngati ticita zinthu mosadzikonda. Conco, kulimbitsa ubwenzi wathu ndi ena kumafuna nthawi komanso khama.

Welengani Miyambo 17:17. Kenako funsani omvela kuti:

  • N’cifukwa ciyani n’canzelu kulimbitsa ubwenzi wathu ndi ena palipano cisautso cacikulu cisanayambe?

Welengani 2 Akorinto 6:​12, 13. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi kugwilitsila nchito mfundo ya pa lembali kungatithandize bwanji kupanga mabwenzi?

Cithunzi ca mu vidiyo yakuti “‘Ciliconse Cili Ndi Nthawi Yake’​​—Kulimbitsa Ubwenzi Kumatenga Nthawi.” August akupatsa Ben bola pamene akhala pa benchi m’bwalo lochailamo basketball.

Tambitsani VIDIYO yakuti “Ciliconse Cili Ndi Nthawi Yake”​—Kulimbitsa Ubwenzi Kumatenga Nthawi. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi vidiyo iyi yakuphunzitsani ciyani pa nkhani ya kulimbitsa ubwenzi?

Ubwenzi uli ngati mbewu imene imafuna kuithilila komanso nthawi yoti ikule. Mungayambitse ubwenzi mwa kumwetulila, kupeleka moni mwansangala, komanso kuwaonetsa cidwi anthu ena. Ndiyeno pang’onom’pang’ono ubwenziwo umakula pamene mupeza nthawi yoceza. Zotulukapo zake n’zakuti mungapange ubwenzi umene ungakhalepo kwamuyaya.

8. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 2 ¶10-18

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 118 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani