LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 September tsa. 2
  • September 1-7

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • September 1-7
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 September tsa. 2

SEPTEMBER 1-7

MIYAMBO 29

Nyimbo 28 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Pewani Miyambo ndi Zikhulupililo Zosagwilizana ndi Malemba

(Mph. 10)

Muzimvela Yehova ndipo mudzakhala ndi cimwemwe ceniceni (Miy. 29:18; wp16.6 6, bokosi)

Pemphani Yehova kuti akupatseni nzelu zokuthandizani kudziwa ngati mwambo winawake ndi wovomelezeka kwa iye (Miy. 29:3a; w19.04 17 ¶13)

Muzikana ngati anthu ena akukukakamizani kucita nawo miyambo yosagwilizana ndi Malemba (Miy. 29:25; w18.11 11 ¶12)

Zithunzi: 1. M’bale akulemba manotsi pomwe akufufuza pogwilitsa nchito Baibo komanso buku lakuti “Malemba Othandiza pa Umoyo Wathu Wacikhristu.” 2. M’bale mmodzimodziyo akuuzako a m’banja lake amene si Mboni zimene amakhulupilila. Ena mwa anthuwo akumvetsela mwachelu pomwe ena akuonetsa kuti akhumudwa ndi zimene m’baleyo akufotokoza.

Kufufuza Malemba mosamala komanso kukamba mwaulemu kungatithandize kuti tisagonje ena akatikakamiza kucita zinthu zosagwilizana ndi Malemba.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Miy. 29:5​—N’cifukwa ciyani tiyenela kuyamikila ena mocokela pansi pa mtima? (w17.10 9 ¶11)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Miy. 29:​1-18 (th phunzilo 5)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) ULALIKI WAMWAYI. Itanilani munthuyo ku nkhani yapadela yotsatila. (lmd phunzilo 2 mfundo 3)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Gwilitsani nchito Nsanja ya Mlonda Na. 1 2025 poyambitsa makambilano. Sinthani ulaliki wanu ngati munthuyo waonetsa cidwi ndi nkhani inayake yosiyana ndi imene munakonzekela. (lmd phunzilo 3 mfundo 3)

6. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 5) ULALIKI WAMWAYI. Gawilani Nsanja ya Mlonda Na. 1 2025 kwa munthu amene waonetsa kuti ali ndi nkhawa cifukwa ca nkhondo. (lmd phunzilo 3 mfundo 4)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 159

7. Zofunikila za Mpingo

(Mph. 15)

8. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30): rr mutu 2 ¶28-31 komanso mabokosi 2A ndi 2B

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 96 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani