LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 November masa. 2-3
  • November 3-9

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • November 3-9
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 November masa. 2-3

NOVEMBER 3-9

NYIMBO YA SOLOMO 1-2

Nyimbo 132 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Nkhani Yokhudza Cikondi Ceniceni

(Mph. 10)

[Onetsani VIDIYO yakuti Mfundo Zokhudza Buku la Nyimbo ya Solomo.]

Solomo anatamanda kwambili mtsikana wa Cisulami ndipo anamulonjeza kuti adzamupatsa zinthu za mtengo wapatali (Nyimbo 1:​9-11)

Cikondi cosatha cimene mtsikana wa Cisulami anali naco pa m’busa n’cimene cinamuthandiza kukhalabe wokhulupilika (Nyimbo 2:​16, 17; w15 1/15 30 ¶9-10)

Mtsikana wa Cisulami akukana ciitano ca Mfumu Solomo kuti apite ku tenti yake. Iye waimilila comupatsa msana atapinda manja. Atumiki atatu a a Solomo aimilila kutsogolo kwa tenti yake ndipo anyamula thaulo, beseni, ndi mtsuko.

ZIMENE MUNGACITE: Pamene mukuwelenga buku la Nyimbo ya Solomo, gwilitsani nchito mbali yakuti “Zimene Zili m’Buku Lino” mu Baibulo la Dziko Latsopano kuti mudziwe amene akulankhula.

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Nyimbo 2:7​—N’cifukwa ciyani mtsikana wa Cisulami ndi citsanzo cabwino kwa Akhristu amene ndi mbeta? (w15 1/15 31 ¶11)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Nyimbo 2:​1-17 (th phunzilo 12)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambilanani naye imodzi mwa mfundo za coonadi zopezeka pa zakumapeto A m’kabuku ka Kondani Anthu. (lmd phunzilo 1 mfundo 3)

5. Kubwelelako

(Mph. 4) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambilanani naye imodzi mwa mfundo za coonadi zopezeka pa zakumapeto A m’kabuku ka Kondani Anthu. (lmd phunzilo 9 mfundo 3)

6. Kupanga Ophunzila

(Mph. 5) lff phunzilo 18 mawu oyamba ndi mfundo 1-3 (th phunzilo 8)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 46

7. “Munthu Wowolowa Manja Adzadalitsidwa”

(Mph. 15) Nkhani yokambilana yokambidwa ndi Mkulu.

Tikamagwilitsa nchito nthawi yathu, mphamvu zathu, ndi zinthu zathu pothandiza ena mowolowa manja timadalitsidwa. Munthu amene walandila thandizo lathu amakhala wosangalala, ndipo nafenso timadalitsidwa cifukwa ca kuolowa manja kwathu. (Miy. 22:9) Tikakhala owolowa manja timakhala acimwemwe podziwa kuti tikutengela citsanzo ca Yehova, ndipo iye adzakondwela nafe.​—Miy. 19:17; Yak. 1:17.

Kamtsikana kakuika copeleka m’bokosi ya zopeleka.
Mwamuna akugwilitsa nchito tabuleti yake kukonza zoti azicita copeleka pa intaneti mwezi uliwonse.

Onetsani VIDIYO yakuti Kupatsa Kumabweletsa Cimwemwe. Kenako funsani omvela kuti:

  • Kodi anthu a mu vidiyoyi apeza bwanji cimwemwe cifukwa ca zopeleka za abale ndi alongo kuzungulila dziko lonse?

  • Nanga apeza bwanji cimwemwe cifukwa copatsa ena mowolowa manja?

Phunzilani Zambili pa Intaneti

Kacizindikilo ka “Zopeleka”, kakuonetsa dzanja la munthu atanyamula ka khobili.

Kodi mungapange bwanji zopeleka zaufulu zothandizila pa nchito ya Mboni za Yehova? Dinizani pa kacizindikilo ka zopeleka kamene kali m’munsi mwa tsamba loyamba pa JW Library®. M’maiko ambili, mukalowa pamenepo mudzapeza polemba kuti FAQ, pomwe pali linki ya dokyumenti yakuti “Donations to Jehovah’s Witnesses​—Frequently Asked Questions”, imene imayankha mafunso amene anthu amafunsa kawilikawili pa nkhani yopanga zopeleka.

8. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 6 ¶1-6 ndi vidiyo ya zimene zili mmutu 6

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 12 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani