LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb25 November masa. 4-5
  • November 10-16

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • November 10-16
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku Misonkhano—2025
mwb25 November masa. 4-5

NOVEMBER 10-16

NYIMBO YA SOLOMO 3-5

Nyimbo 31 ndi Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kukongola kwa Umunthu Wamkati N’kofunika Kwambili

(Mph. 10)

Zokamba za mtsikana wa Cisulami zinaonetsa kukongola kwa umunthu wake wamkati (Nyimbo 4:​3, 11; w15 1/15 30 ¶8)

Khalidwe lake loyela analiyelekezela ndi munda wokongola kwambili (Nyimbo 4:12; w00-CN 11/1 11 ¶17)

Kukhala ndi makhalidwe abwino n’kofunika kwambili kuposa kukhala wokongola, ndipo tonse tingathe kukhala ndi makhalidwe amenewa (g04-CN 12/22 9 ¶2-5)

Zithunzi: 1. Mwacikondi, mlongo wacikulile akulimbikitsa mlongo wacitsikana amene akuvutika kwambili maganizo. 2. Mwacimwemwe, m’bale wacinyamata akuthandiza m’bale wacikulile pamene akugwilila nchito limodzi mu utumiki.

DZIFUNTSENI KUTI, ‘Kodi ndi makhalidwe ati amene ndimakonda kwambili mwa ena?’

2. Kufufuza Cuma Cauzimu

(Mph. 10)

  • Nyimbo 3:5​—N’cifukwa ciyani “ana aakazi a ku Yerusalemu” anawalumbilitsa “pali insa ndiponso pali mphoyo zakuchile”? (w06-CN 11/15 18 ¶4)

  • Pa kuwelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?

3. Kuwelenga Baibo

(Mph. 4) Nyimbo 4:​1-16 (th phunzilo 2)

CITANI KHAMA PA ULALIKI

4. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 3) KUNYUMBA NDI NYUMBA. M’pempheni kuti muyambe kuphunzila naye Baibo. (lmd phunzilo 6 mfundo 4)

5. Kuyambitsa Makambilano

(Mph. 4) ULALIKI WAMWAYI. Muonetseni mmene angapezele nkhani m’cinenelo cake pa jw.org. (lmd phunzilo 4 mfundo 3)

6. Nkhani

(Mph. 5) ijwbq nkhani 131​—Mutu: Kodi Baibo Imati Ciyani pa Nkhani Yophauda Komanso Kuvala Zodzikongoletsela? (th phunzilo 1)

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo 36

7. Kukwatila Kokha mwa Ambuye (Gen. 28:2)

(Mph. 8)

Onetsani VIDIYO.

8. Kodi Mudzakhala Mwamuna Kapena Mkazi Wabwino?

(Mph. 7) Kukambilana.

Kodi mukufunafuna munthu womanga naye banja? Kodi ndi makhalidwe ati amene mumafuna mwa munthu amene mukufuna kumanga naye banja? Kodi Akhristu ena amene nawonso akufunafuna munthu womanga naye banja amaona kuti muli ndi makhalidwe abwino? Nthawi zina, munthu angamacite zinthu monga wauzimu, koma m’kupita kwa nthawi umunthu wake wamkati umaonekela.

Mlongo akuuza mayi wacikulile kuti akhale pa mpando umene iye anakhala mu basi.
M’bale akugawila ka thilakiti kwa wanchito mnzake pamene akucoka pamalo amene anali kugwilila nchito.
Abale awili ndi alongo awili akugwilila nchito limodzi mu utumiki. M’modzi mwa abalewo akuuza alongo za kumalo kumene ayenela kukalalikila.

Lembani lemba logwilizana ndi khalidwe lililonse limene munthu wauzimu amaonetsa.

  • Kukonda Yehova ndi kumukhulupilila

  • Kukhala mutu wa banja wabwino kapena kukhala mkazi wogonjela

  • Wosadzikonda komanso wodzimana

  • Woganiza bwino komanso wololela

  • Wakhama komanso wolimbikila pa nchito

9. Phunzilo la Baibo la Mpingo

(Mph. 30) rr mutu 6 ¶7-13 ndi bokosi 6A

Mawu Othela (Mph. 3) | Nyimbo 70 ndi Pemphelo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani