LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w24 March tsa. 32
  • Kukhululuka Macimo Dipo Lisanapelekedwe

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kukhululuka Macimo Dipo Lisanapelekedwe
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
  • Nkhani Zofanana
  • Dipo la Yesu—Mphatso ya Mulungu Yopambana Zonse
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Dipo Ni Mphatso Ya Mulungu Yopambana Zonse
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Pitilizani Kuyamikila Dipo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2021
  • Dipo—‘Mphatso Yangwilo’ Yocokela kwa Atate
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
w24 March tsa. 32

MAWU A M’BAIBO

Kukhululuka Macimo Dipo Lisanapelekedwe

Mulungu amatikhululukila macimo athu kokha kupitila mu nsembe ya dipo ya magazi a Yesu. (Aef. 1:7) Koma Baibo imati: “Mulungu anacita izi pofuna kuonetsa cilungamo cake pokhululuka macimo amene anacitika kale,” kutanthauza Yesu asanapeleke dipo. (Aroma 3:25) Kodi zinatheka bwanji Yehova kucita zimenezi, koma pa nthawi imodzi-modzi akusungabe cilungamo cake?

Yehova atalonjeza kuti adzapeleka “mbewu” imene idzapulumutsa anthu omukhulupilila, kwa Iye zinali ngati nsembe ya dipo yapelekedwa kale. (Gen. 3:15; 22:18) Mulungu anali wotsimikiza ndithu kuti Mwana wake wobadwa yekha adzapeleka dipo mofunitsitsa. (Agal. 4:4; Aheb. 10:​7-10) Yesu ali pa dziko lapansi monga woimilako Yehova, anali na mphamvu zokhululukila macimo dipo isanapelekedwe. Anacita zimenezi kwa omwe anam’khulupilila podziŵa kuti dipo limene anali kudzapeleka inali kudzaphimba macimo awo.—Mat. 9:​2-6

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani