LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 June tsa. 32
  • Kukumbukila Malemba

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kukumbukila Malemba
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Nkhani Zofanana
  • Mmene Tingaseŵenzetsele JW Laibulale
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Kachulidwe ka Malemba Koyenela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Laibulali Imene Mungathe Kuinyamula Kumanja
    Mmene Zopeleka Zanu Zimagwilila Nchito
  • Kumveketsa Bwino Cifukwa Coŵelengela Lemba
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 June tsa. 32

MFUNDO YOTHANDIZA PA KUWELENGA KWANU

Kukumbukila Malemba

Kodi munavutikapo kukumbukila lemba limene mumakonda? Lembalo lingakhale limene limakutonthozani kapena kukuthandizani kugonjetsa maganizo olakwika. Mwina ndi limene munali kufuna kuuzako wina. (Sal. 119:​11, 111) Nazi njila zina zimene zingakuthandizeni kukumbukila malemba.

  • Gwilitsani nchito JW Library®. Pangani tag (tagi)a n’kuipatsa dzina lakuti “Malemba Apamtima.” Muziika malemba amene mufuna kukumbukila mu tagi imeneyi.

  • Ikani lembalo pamene mungamalione mosavuta. Mungalembe vesi limene mukufuna kumakumbukila pa pepala, n’kuika pepalalo pamalo amene mungalione kawilikawili. Ena amaika lembalo pafupi ndi galasi yodziyang’anilapo, ndipo enanso amaika pa citseko ca filiji. Ndipo ena amajambula cithunzi ca lembalo n’kuciika pa sikilini ya kompyuta yawo kapena pa foni.

  • Gwilitsani nchito pepala. Mungalembe lembalo kumbali imodzi ya pepala ndi kulemba mawu ake kumbali inayo. Yesani kuona mawuwo n’kukumbukila lembalo, kapena kuona lemba n’kukumbukila mawu ake, kapenanso mungaone mawuwo n’kuyesa kukumbukila kumene lembalo limapezeka m’Baibo.

a Kuti mudziwe zambili pa nkhani ya matagi, penyelelani vidiyo yakuti Zimene Gulu Likukwanilitsa​—Mfundo Zothandiza Poseŵenzetsa JW Library pa jw.org.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani