LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 November tsa. 32
  • Kusewenzetsa ‘Mphatso Yanu Yauzimu’

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kusewenzetsa ‘Mphatso Yanu Yauzimu’
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Nkhani Zofanana
  • ‘Pitilizani Kulimbikitsana Tsiku na Tsiku’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
  • Kusakila Mphatso Yabwino Koposa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Mphatso ya Mulungu Yopambana Zonse N’cifukwa Ciani ni Yamtengo Wapatali?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • “Inali Mphatso Yabwino Koposa Imene Sin’nalandilepo”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 November tsa. 32

MAU A M’BAIBO

Kusewenzetsa ‘Mphatso Yanu Yauzimu’

Tonsefe timalimbikitsidwa tikakhala pamodzi ndi abale komanso alongo. Koma kuti nthawi imeneyi izikhaladi yolimbikitsa, pali zina zimene tiyenela kucita. M’Baibo, kulimbitsa cikhulupililo ca wina ndi mnzake kumachedwa “mphatso . . . yauzimu.” (Aroma 1:​11, 12) Kodi mphatsoyi tingaigwilitse nchito bwanji mokwanila?

Limbikitsani ena mwa mau anu. Mwacitsanzo, tingalimbikitse ena pamisonkhano mwa kupeleka ndemanga zokamba kwambili za Yehova, Mau ake, ndi anthu ake, osati za ife. Ndipo poceza ndi alambili anzathu, tiyenela kukambilana nkhani zolimbikitsa.

Limbikitsani ena mwa zisankho ndi zocita zanu. Mwacitsanzo, ena apanga cisankho cokhalabe mu utumiki wanthawi zonse ngakhale kuti akukumana ndi mabvuto enaake. Ena amafika pamsonkhano wa mkati mwa mlungu ngakhale kuti amapanikizika ndi nchito, kapena akudwala matenda osathelapo.

Kodi mau ndi zocita zanu zimalimbikitsa abale ndi alongo anu? Ndipo kodi mumakhala chelu kuti muone zimene ena amakamba ndi kucita kuti akulimbikitseni?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani