LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 December tsa. 32
  • Limbitsani Cikhulupililo Canu Cakuti Yehova Ali ndi Mphamvu Zokupulumutsani

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Limbitsani Cikhulupililo Canu Cakuti Yehova Ali ndi Mphamvu Zokupulumutsani
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Nkhani Zofanana
  • N’zotheka Kuti Muziwadalila Abale Anu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Kodi Mumakhulupilila Mmene Yehova Amacitila Zinthu?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Kodi Mudzacita Ciani pa Nthawi ya Cilala?
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • “Inu Mulungu Wanga, Cikhulupililo Canga Cili mwa Inu”
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 December tsa. 32

ZIMENE MUNGACITE PA KUWELENGA KWANU

Limbitsani Cikhulupililo Canu Cakuti Yehova Ali ndi Mphamvu Zokupulumutsani

Welengani Numeri 13:25–14:4 imene ionetsa kuti Aisiraeli sanali kum’khulupilila Yehova.

Mvetsani nkhani yonse. N’cifukwa ciani Aisiraeli pamene anali kucoka ku Iguputo anali kufunika kukhala ndi cikhulupililo cakuti Yehova ali ndi mphamvu zowapulumutsa? (Sal. 78:​12-16, 43-53) N’ciani cinawalepheletsa kum’dalila Yehova? (Deut. 1:​26-28) Kodi Yoswa ndi Kalebe anaonetsa bwanji kuti anali kum’dalila Yehova?​—Num. 14:​6-9.

Kumbani mozamilapo. Kodi Aisiraeli anayenela kutani kuti azim’dalila kwambili Yehova? (Sal. 78:​12-16, 43-53) Kodi pali kugwilizana kotani pakati pa kudalila Yehova ndi kum’lemekeza?​—Num. 14:11.

Ganizilani zimene mungaphunzilepo. Dzifunseni kuti:

  • ‘Ndi pa zocitika ziti pomwe zingakhale zobvuta kwa ine kudalila Yehova ndi mtima wonse?’

  • ‘Ndingatani kuti ndizim’dalila kwambili Yehova pali pano komanso m’tsogolo?’

  • ‘Cisautso cacikulu cikadzayamba, kodi n’ciani cimene sindiyenela kukaikila ngakhale pang’ono?’​—Luka 21:​25-28.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani