THANDIZO KWA OFEDWA
Kuŵaŵa Kwa Imfa
“Tinali titakhala m’cikwati kwa zaka zopitilila 39, pamene mkazi wanga Sophiaa anamwalila pambuyo podwala kwa nthawi yaitali. Anzanga ananithandiza kwambili, ndipo n’nali kudzitangwanitsa na zocita zambili. Koma kwa caka conse, n’navutika kwambili na cisoni. N’nali kuti nikakhalako bwino kwa kanthawi, cisoni n’kunibwelelanso. Ngakhale kuti papita zaka pafupi-fupi zitatu kucokela pamene anamwalila, nthawi zina nimagwidwa na cisoni kwambili.”—Kostas.
Kodi munataikilidwapo wokondedwa wanu mu imfa? Ngati munataikilidwapo, mungavomeleze zimene Kostas anakamba. Imfa ya mnzako wa m’cikwati, m’bululu wako, kapena mnzako wapamtima, imavutitsa kwambili maganizo na kuŵaŵitsa mtima. Ngakhale akatswili ofufuza za anthu ofedwa amavomeleza mfundo imeneyi. Nkhani ya m’magazini yakuti, The American Journal of Psychiatry, imati “imfa ni yoŵaŵa kwambili ndipo imabweletsa cisoni cosathelapo.” Cifukwa ca cisoni cacikulu ca imfa, munthu wofedwa angafunse kuti: ‘Kodi cisoni cimeneci cidzatha liti? Kodi nidzakhalanso wacimwemwe? Kodi ningapeze kuti citonthozo?’
Mudzapeza mayankho pa mafunso amenewa m’magazini ino ya Galamuka! Nkhani yotsatila idzafotokoza zimene mungayembekezele ngati posacedwa wokondedwa wanu anamwalila. Ndipo nkhani zina zokonkhapo zidzafotokoza njila zimene zingakuthandizeni kucepetsako cisoni mukafedwa.
Tikhulupilila kuti nkhani zotsatila zidzathandiza aliyense amene anataikilidwa wokondedwa wake mu imfa.
a Maina ena m’nkhani za m’magazini ino asinthidwa.