LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g22 na. 1 masa. 10-12
  • 3 | Tetezani Ubale Wanu na Ena

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • 3 | Tetezani Ubale Wanu na Ena
  • Galamuka!—2022
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • CIFUKWA CAKE KUCITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA
  • Zimene Muyenela Kudziŵa
  • Zimene Mungacite Pali Pano
  • Sankhani Anzanu Mwanzelu
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • M’kope Ino ya Galamuka!
    Galamuka!—2022
  • Inu Makolo—Thandizani Ana Anu Kukonda Yehova
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
  • Makolo—Phunzitsani Ana Anu Kukonda Yehova
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
Onaninso Zina
Galamuka!—2022
g22 na. 1 masa. 10-12
Mwamuna na mkazi wake, omwe ni acikulile komanso osangalala, akumbatilana.

DZIKOLI LILI PA MAVUTO AAKULU

3 | Tetezani Ubale Wanu na Ena

CIFUKWA CAKE KUCITA ZIMENEZI N’KOFUNIKA

Pamene nkhawa ikula cifukwa ca mavuto a m’dzikoli, mosadziŵa anthu ambili amalola ubale wawo na anthu ena kusokonezeka.

  • Anthu amadzipatula kwa mabwenzi awo.

  • Anthu okwatilana amangokangana-kangana.

  • Makolo sakhala na cidwi kwenikweni cofuna kudziŵa nkhawa za ana awo.

Zimene Muyenela Kudziŵa

  • Mabwenzi ni ofunika kwambili cifukwa amatithandiza kukhala na thanzi labwino, komanso kukhala olimba makamaka tikakumana na mavuto.

  • Nkhawa yobwela cifukwa ca mavuto a m’dzikoli, ingakhudze kwambili umoyo wa banja lanu.

  • Ana akamva kapena kuona zinthu zoopsa pa nyuzi, angacite mantha kwambili kuposa mmene mungaganizile.

Zimene Mungacite Pali Pano

Baibo imati: “Bwenzi lenileni limakukonda nthawi zonse, ndipo bwenzilo ndi m’bale amene anabadwila kuti akuthandize pakagwa mavuto.”—Miyambo 17:17.

Mabwenzi angatithandize na kutipatsa ulangizi wabwino. Kungodziŵa kuti munthu wina wake amasamala za ife kungatithandize kuti tipilile mavuto a tsiku na tsiku.

ZIMENE MUNGACITE​—Mfundo Zothandiza

Pa nthawi ya mavuto aakulu, tetezani ubale wanu na anthu amene mumakonda mwa kucita izi

LIMBITSANI UKWATI WANU

Mwamuna na mkazi wake, omwe ni acikulile komanso osangalala, akumbatilana.

Kulimbitsa ukwati wanu

Baibo imati: “Aŵili amaposa mmodzi . . . Ngati mmodzi wa iwo atagwa, winayo akhoza kum’dzutsa mnzakeyo.” (Mlaliki 4:9, 10) Anthu okwatilana ayenela kukhala ngati woyendetsa ndeke na womuthandiza wake, amene ali na colinga copita ku malo amodzi, osati ngati ndeke ziŵili za nkhondo zimene zifuna kuwombana.

  • Tsimikizani mtima kuti muzicitabe zinthu mokoma mtima na mnzanu wa mu ukwati ngakhale pamene mwapanikizika na mavuto. Kukhala woleza mtima komanso wololela n’kothandiza kwambili.

  • Kamodzi pa mlungu, muzikambilanako na mwamuna kapena mkazi wanu za mavuto amene muyenela kuwathetsa. Kumbukilani kuti colinga canu ni kuthana na mavutowo osati kuimba mlandu mnzanuyo.

  • Muzipatulako nthawi yocitila pamodzi zinthu zimene nonse aŵili mumakonda.

  • Muzikumbukila zinthu zosangalatsa zimene munacitila pamodzi. Mwacitsanzo, mungapatuleko nthawi yoona zithunzi za pa cikwati canu kapena za pa cocitika cina cosangalatsa.

“Mwamuna na mkazi wake sangagwilizane pa ciliconse, koma izi sizitanthauza kuti sangacitile zinthu pamodzi. Iwo angapangile limodzi cisankho na kuthandizana kuti akwanilitse zimene asankhazo.”—David.

KHALANIBE PA UBALE WABWINO NA ENA

  • Azimayi osiyana mitundu akuseka na kusangalala na maceza.

    Kulimbitsa ubale wanu na ena

    Musamangoganizila mmene mabwenzi anu angakuthandizileni, koma muziganizilanso mmene inuyo mungathandizile ena. Mukamalimbikitsa ena, inunso mumalimbikitsidwa.

  • Tsiku lililonse, muzikambilanako na anzanu ena kuti mudziwe za umoyo wawo.

  • Afunseni kuti akuuzeni zimene zimawathandiza kupilila mavuto ofanana na amene inu mukukumana nawo.

“Munthu ukakumana na mavuto aakulu, umakhala ngati uli mumdima. Mabwenzi angakuthandize kudziŵa pamene uli komanso kumene uyenela kuloŵela. Angacite zimenezi mwina mwa kungokukumbutsa zinthu zimene ukuzidziŵa kale. Mabwenzi amakukonda, ndipo amadziŵa kuti nawenso umawakonda.”—Nicole.

MUZILIMBIKITSA ANA ANU

Makolo na ana awo aŵili akhala pa dooko, ndipo akuyang’ana mwacidwi malo okongola a m’mbali mwa nyanja.

Kulimbikitsa ana anu

Baibo imati: “Munthu aliyense akhale wofulumila kumva, wodekha polankhula.” (Yakobo 1:19) Poyamba, ana anu sangakhale omasuka kufotokoza zimene amaopa kapena kuda nazo nkhawa. Koma mukamawamvetsela moleza mtima, mungawathandize kukhala omasuka.

  • Muzicitako zinthu zimene zingathandize ana anu kukhala omasuka kukamba za kumtima kwawo. Ana ena sakhala omasuka kulankhula ngati mwacita kukhala nawo pansi kuti mukambilane nawo. Koma amakhala omasuka ngati mucita nawo zinthu zina monga kuyenda pa motoka kapena pansi.

  • Onetsetsani kuti ana anu samvetsela kapena kuonelela kwambili nkhani zocititsa mantha.

  • Auzeni ana anu zimene mwakonza kuti muteteze banja lanu.

  • Konzekelani zoyenela kucita pakagwa tsoka, ndipo yesezani zimenezo pamodzi ndi ana anu.

“Muzikambilana na ana anu, na kuwalola kufotokoza mmene akumvela. Iwo angakhale na mantha, nkhawa, kapena mkwiyo, koma osamasuka kufotokoza. Auzeni kuti inunso mumamva cimodzimodzi nthawi zina, ndipo afotokozeleni zimene zimakuthandizani mukamva conco.”—Bethany.

Cithunzi ca mu vidiyo yakuti “N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe.” Mwamuna na mkazi wake osangalala agwilana manja, ndipo akuyenda mumsewu.

KUTI MUDZIŴE ZAMBILI, onelelani vidiyo yakuti N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani