LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • fg phunzilo 6 Mafunso. 1-5
  • Kodi Tili ndi Ciyembekezo Canji Ponena za Akufa?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Tili ndi Ciyembekezo Canji Ponena za Akufa?
  • Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Nkhani Zofanana
  • Ciyembekezo Cotsimikizilika Cakuti Okondedwa Athu Amene Anamwalila Adzauka
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Kodi Munthu Akamwalila, Cimacitikano N’ciyani?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Akufa Adzauka Ndithu!
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
Onaninso Zina
Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
fg phunzilo 6 Mafunso. 1-5

PHUNZILO 6

Kodi Tili ndi Ciyembekezo Canji Ponena za Akufa?

1. Kodi uthenga wabwino pankhani ya akufa ni wakuti bwanji?

Marita ndi Mariya akulandila mlongo wao Lazaro kucokela kwa akufa

Yesu atafika ku Betaniya pafupi ndi Yerusalemu, panali patapita masiku anai kucokela pamene bwenzi lake Lazaro anamwalila. Yesu anapita kumanda a Lazaro pamodzi ndi Malita ndi Mariya, alongosi a womwalilayo. Posapita nthawi, anthu anasonkhana. Malita ndi Mariya anasangalala kwambili pamene Yesu anaukitsa Lazaro.​—Ŵelengani Yohane 11:21-24, 38-44.

Malita anali kudziŵa kale zimene uthenga wabwino unanena za akufa. Iye anali kudziŵa kuti Yehova adzaukitsa akufa kuti adzakhalenso ndi moyo padziko lapansi.​—Ŵelengani Yobu 14:14, 15.

2. Kodi akufa ali mu mkhalidwe wabwanji?

Kulengedwa kwa Adamu, kenako imfa yake

Mulungu anauza Adamu kuti: “Popeza ndiwe fumbi, kufumbiko udzabwelela.”—GENESIS 3:19.

Anthu anapangidwa ndi dothi. (Genesis 2:7; 3:19) Sindife mizimu imene ili m’thupi lanyama. Koma ndife zolengedwa zokhala ndi thupi lanyama, ndipo tikamwalila palibe ciliconse cimene cimapitiliza kukhala ndi moyo. Tikafa, ubongo wathu naonso umafa, ndipo timaleka kuganiza. N’cifukwa cake pamene Lazaro anaukitsidwa sanakambe ciliconse cokhudza mkhalidwe wa akufa cifukwa io sadziŵa ciliconse.​—Ŵelengani Salimo 146:4; Mlaliki 9:5, 6, 10.

Kodi Mulungu amazunza anthu m’moto akamwalila? Popeza kuti Baibo imaonetsa kuti akufa sadziŵa ciliconse, n’zoonekelatu kuti ciphunzitso ca moto wa kuhelo n’cabodza. Cimaipitsa dzina la Mulungu. Mulungu sangaganize zozunza anthu m’moto cifukwa cakuti maganizo amenewo ni oipa kwambili.​—Ŵelengani Yeremiya 7:31.

Tambani vidiyo Kodi Akufa Ali mu Mkhalidwe Wabwanji?

3. Kodi akufa angakambe ndi ife?

Akufa sangakambe kapena kumva. (Salimo 115:17) Koma pali angelo oipa, amene amatha kukamba kwa anthu ndi kuyelekezela kuti ndi anthu amene anamwalila. (2 Petulo 2:4) Yehova amatiletsa kufunsila kwa akufa.​—Ŵelengani Deuteronomo 18:10, 11.

4. Kodi ndani adzaukitsidwa?

Munthu amene anaukitsidwa kukhala ndi moyo m’paladaiso aphunzila za Mulungu. Ndiyeno munthuyo aphunzitsako ena amene aukitsidwa.

Anthu akufa mamiliyoni ambili amene ali m’manda adzakhalanso ndi moyo padziko lapansi. Ngakhale ena amene sanadziŵe Mulungu ndipo anali kucita zoipa adzaukitsidwa.​—Ŵelengani Luka 23:43; Machitidwe 24:15.

Anthu amene adzaukitsidwa adzaphunzila coonadi ca Mulungu ndi kuonetsa cikhulupililo mwa Yesu mwa kumumvela. (Chivumbulutso 20:11-13) Anthu amene adzakhalanso ndi moyo ndi kucita zinthu zabwino adzakhala ndi moyo wamuyaya padziko lapansi.​—Ŵelengani Yohane 5:28, 29.

5. Kodi ciukililo cimatiuza ciani za Yehova

Ciyembekezo cakuti akufa adzauka cidzakwanilitsidwa cifukwa cakuti Mulungu anatumiza Mwana wake kuti adzatifele. Mwa ici, ciukililo cimatiuza za cikondi ca Yehova ndi cisomo cake. Pamene akufa adzauka, ndani maka-maka amene mudzafuna kuona?​—Ŵelengani Yohane 3:16; Aroma 6:23.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 6, 7, ndi 10 m’buku lakuti Zimene Baibo Imaphunzitsa m’Ceni-ceni.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani