LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w13 10/1 tsa. 32
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Nkhani Zofanana
  • Kuyankha Mafunso A M’baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Kodi Tili ndi Ciyembekezo Canji Ponena za Akufa?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kodi Ciukitso N’ciyani?
    Kuyankha Mafunso Okhudza Baibo
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
w13 10/1 tsa. 32

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBO

Kodi akufa adzakhalanso ndi moyo?

Imfa ili ngati tulo cifukwa cakuti munthu wakufa palibe cimene amadziŵa ndipo sangacite ciliconse. Koma Mlengi wa moyo angathe kuukitsa akufa. Mulungu anaonetsa kuti angathe kucita zimenezi mwa kupatsa Yesu mphamvu kuti aukitse anthu angapo akufa.—Ŵelengani Mlaliki 9:5; Yohane 11:11, 43, 44.

Mulungu walonjeza kuti adzaukitsa anthu amene akuwakumbukila kuti adzakhale ndi moyo padziko lapansi latsopano. Anthu akufa ali kumanda kuyembekezela nthawi imene Mulungu adzawaukitsa. Mulungu Wamphamvuyonse amalaka-laka kuukitsa anthu amene anafa.—Ŵelengani Yobu 14:14, 15.

Kodi ciukililo cidzacitika bwanji?

Anthu amene Mulungu adzaukitsa adzakwanitsa kudzidziŵa io eni. Adzakwanitsanso kudziŵa mabwenzi ao ndi acibanja ao. Ngakhale kuti anthu akafa matupi ao amaola, Mulungu sangalephele kuukitsa anthu amenewo ndi matupi atsopono.—Ŵelengani 1 Akorinto 15:35, 38.

Anthu ocepa amaukitsidwa ndi kupita kumwamba. (Chivumbulutso 20:6) Anthu ambili amene adzaukitsidwa adzakhala ndi moyo padziko lapansi la paladaiso. Iwo adzakhala ndi umoyo watsopano ndiponso mwai wokhala ndi moyo wamuyaya.—Ŵelengani Salimo 37:29; Machitidwe 24:15.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 6 ndi 7 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

[Cithunzi papeji 32]

Kodi imfa imafanana bwanji ndi tulo?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani