LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • T-34 masa. 1-4
  • Kodi Mavuto Adzathadi?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Mavuto Adzathadi?
  • Kodi Mavuto Adzathadi?
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
    Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
  • Kodi N’zoona Kuti Akufa Angakhalenso ndi Moyo?
    Kodi N’zoona Kuti Akufa Angakhalenso ndi Moyo?
  • Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Ciani?
    Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Ciani?
  • Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli?
    Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli
Onaninso Zina
Kodi Mavuto Adzathadi?
T-34 masa. 1-4

Kodi Mavuto Adzathadi?

Kodi mwayankha kuti . . .

  • inde?

  • iyai?

  • kaya?

ZIMENE BAIBO IMANENA

“Mulungu . . adzapukuta misozi yonse m’maso mwao, ndipo imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulila, kapena kubuula, ngakhale kupweteka.”—Chivumbulutso 21:3, 4, Baibulo la Dziko Latsopano.

UBWINO WOKHULUPILILA ZIMENEZI

Mudzavomeleza kuti si Mulungu amene amacititsa mavuto.—Yakobo 1:13.

Mudzasangalala kudziŵa kuti Mulungu amakhudzidwa tikakumana ndi mavuto.—Zekariya 2:8.

Mudzakhala ndi ciyembekezo cakuti mavuto onse adzatha.—Salimo 37:9-11.

Mwamuna akuŵelenga Baibo ndipo akuganizila za kutha kwa mavuto ndi kupanda cilungamo padziko.

KODI TINGAKHULUPILILEDI ZIMENE BAIBO IMANENA?

Inde, pa zifukwa ziŵili izi:

  • Mulungu amadana ndi mavuto ndi kupanda cilungamo. Ganizilani mmene Yehova Mulungu anamvelela pamene anthu ake akale anacitilidwa nkhanza. Baibo imakamba kuti iye anavutika mtima pamene adani ake anali ‘kukankha-kankha’ anthu ake.—Oweruza 2:18, Baibulo la Dziko Latsopano.

    Mulungu amadana kwambili ndi anthu amene amakonda kuvulaza anzao. Mwacitsanzo, Baibo imakamba kuti Mulungu amanyansidwa ndi “manja okhetsa magazi a anthu osalakwa.”—Miyambo 6:16, 17.

  • Mulungu amadela nkhawa aliyense wa ife. Si munthu yekha amene amadziŵa “mlili wake ndi ululu wake,” koma Yehova nayenso amadziŵa zimenezo.—2 Mbiri 6:29, 30.

    Kupyolela mu Ufumu wake, Yehova posacedwapa adzacotsapo mavuto amene munthu aliyense ali nao. (Mateyu 6:9, 10) Koma pakali pano, iye amatonthoza anthu onse amene amam’funa-funa.—Machitidwe 17:27; 2 Akorinto 1:3, 4.

GANIZILANI FUNSO ILI

Akazi aŵili akuphunzila Baibo

N’cifukwa ciani Mulungu amalola kuti tizivutika?

Baibo imayankha funso limeneli pa AROMA 5:12 ndi pa 2 PETULO 3:9.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani