LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 11/1 tsa. 16
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’ciani?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Kodi Ufumu Wa Mulungu N’ciani?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’ciani?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Kodi Baibulo Imakamba Ciani?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 11/1 tsa. 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

N’cifukwa ciani tiyenela kupemphela kuti Ufumu wa Mulungu ubwele?

Ufumu wa Mulungu ndi boma la kumwamba. Yesu anauza ophunzila ake kupemphela kuti ufumuwo ubwele, cifukwa udzabwezeletsa cilungamo ndi mtendele padziko lapansi. Kulibe boma la anthu limene lingathetseletu nkhanza, kupanda cilungamo kapena matenda. Koma Ufumu wa Mulungu ndi umene ungakwanitse ndipo udzacitadi zimenezi. Mulungu wasankha Yesu Mwana wake kukhala Mfumu ya Ufumu umenewo. Yehova wasankhanso gulu la otsatila a Yesu kuti akakhale olamulila anzake mu Ufumuwo.—Ŵelengani Luka 11:2; 22:28-30.

Posacedwapa, Ufumu wa Mulungu udzacotsapo anthu onse amene amatsutsa ulamulilo wa Mulungu. Conco, tikamapemphela kuti Ufumu wa Mulungu ubwele timakhala kuti tikupempha kuti boma la Mulungu liloŵe m’malo mwa maboma a anthu.—Ŵelengani Danieli 7:13, 14; Chivumbulutso 11:15, 18.

N’cifukwa ciani anthu adzapindula ndi Ufumu wa Mulungu?

Yesu ndi Mfumu yoyenelela cifukwa ndi wacifundo. Pokhala Mwana wa Mulungu, iye alinso ndi mphamvu zothandiza anthu amene amafuulila Mulungu pofuna thandizo.—Ŵelengani Salimo 72:8, 12-14.

Ufumu wa Mulungu udzapindulitsa makamaka anthu onse amene amaupemphelela ndi mtima wonse komanso amene amacita zinthu mogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu. Kuphunzila zimene Baibulo limanena zokhudza Ufumu wa Mulungu ndi kosangalatsa.—Ŵelengani Luka 18:16, 17; Yohane 4:23.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 17 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Buku limeneli lipezekanso pa Webusaiti ya www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani