LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 February tsa. 3
  • Fanizo la Tiligu ndi Namsongole

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Fanizo la Tiligu ndi Namsongole
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • “Dziŵani Kuti Ine Ndili Pamodzi Ndi Inu masiku Onse”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • “Ufumu Wanu Ubwele”
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 February tsa. 3

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | MATEYU 12-13

Fanizo la Tiligu ndi Namsongole

Yesu anaseŵenzetsa fanizo la tiligu ndi namsongole pofuna kuonetsa mmene adzatengela gulu lonse la Akhristu odzozedwa pakati pa anthu, ndi kuti Akhristuwo adzayamba kudzozedwa kuyambila mu 33 C.E.

Nthawi yofesa, yokolola, na yosonkhanitsila m’nkhokwe

13:24

‘Munthu anafesa mbewu zabwino m’munda mwake’

  • Wofesa: Yesu Khristu

  • Mbewu zabwino zifesedwa: Ophunzila a Yesu adzozedwa na mzimu woyela

  • Munda: Anthu onse pa dziko lapansi

13:25

“Anthu ali m’tulo, kunabwela mdani wake. Mdaniyo anafesa namsongole”

  • Mdani: Mdyelekezi

  • Anthu ali m’tulo: Imfa ya atumwi

13:30

“Zilekeni zonse zikulile pamodzi mpaka nthawi yokolola”

  • Tiligu: Akhristu odzozedwa

  • Namsongole: Akhristu onama

“Coyamba sonkhanitsani namsongole . . . ; Mukatha mupite kukasonkhanitsa tiligu”

  • Akapolo/okolola: Angelo

  • Kusonkhanitsidwa kwa Namsongole: Kucotsewa kwa Akhristu onama pakati pa Akhristu odzozedwa

  • Kusonkhanitsila m’nkhokwe: Akhristu odzozedwa asonkhanitsidwa mumpingo umene unakhazikitsidwanso

Pamene nyengo yokolola inayamba, n’ciani cinasiyanitsa Akhristu oona na Akhristu onama?

Kodi kumvetsetsa fanizo ili kunganipindulitse bwanji ine panekha?

KODI MUDZIŴA?

Tiligu ndi namsongole zikulila pamodzi

Anthu ena amakhulupilila kuti namsongole wa m’fanizo ili anali udzu woipa wochedwa bearded darnel. Udzu umenewu ni poizoni ndipo umaoneka wofanana kwambili na tiligu maka-maka ngati sunakhwime. Ngati tiligu ndi namsongole zikulila pamodzi, mizu yake imalukana-lukana, ndipo zikakhala conco zimakhala zovuta kunyula namsongole popanda kunyula tiligu. Koma ngati namsongole wakhwima, sizikhala zovuta kumuzindikila na kumucotsa.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani