LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 February tsa. 5
  • Kudyetsa Anthu Ambili Mwa Kugwilitsila Nchito Anthu Ocepa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kudyetsa Anthu Ambili Mwa Kugwilitsila Nchito Anthu Ocepa
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Kudyetsa Anthu Ambili Mwa Kugwilitsila Nchito Anthu Ocepa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • “Ndani Kweni-kweni Amene Ali Kapolo Wokhulupilika Ndi wanzelu?”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • “Kumbukilani Amene Akutsogolela Pakati Panu”
    Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
  • Kodi Kapolo Wokhulupilika ndi Wanzelu Ndani?
    Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano?
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 February tsa. 5
Ophunzila a Yesu adyetsa khamu la anthu

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | MATEYU 14-15

Kudyetsa Anthu Ambili Mwa Kugwilitsila Nchito Anthu Ocepa

Pasika wa mu 32 C.E. ali pafupi kucitika, Yesu anacita cozizwitsa cimene olemba Mauthenga Abwino onse anayi anacilemba.

Mwa cozizwitsa cimeneco, Yesu anakhazikitsa njila kapena kuti chanelo imene akuigwilitsilabe nchito masiku ano.

14:16-21

  • Yesu anauza ophunzila ake kuti adyetse khamu la anthu, ngakhale kuti anali cabe na mitanda isanu ya mkate na nsomba ziŵili

  • Yesu atatenga mitanda ya mkate na nsomba zija, anapemphela. Kenako, anagaŵila ophunzila ake, amenenso anagaŵila khamu la anthu

  • Mozizwitsa, panakhala cakudya cokwanila aliyense kudya na kutsalako. Yesu anadyetsa anthu masauzande mwa kugwilitsila nchito anthu ocepa—ophunzila ake

    Yesu agaŵila cakudya kwa ophunzila ake; Nsanja ya Mlonda
  • Yesu anakambilatu kuti m’masiku otsiliza, adzakhazikitsa njila kapena kuti chanelo yopelekela cakudya cauzimu “pa nthawi yoyenela.”—Mat. 24:45

  • Mu 1919, Yesu anasankha “kapolo wokhulupilika ndi wanzelu,” kagulu kocepa ka abale odzozedwa, kuti aziyang’anila “anchito ake apakhomo,” amene amapatsidwa cakudya ca kuuzimu

  • Kupitila m’kagulu kocepa kameneka ka abale odzozedwa, Yesu akutsatila njila imene anakhazikitsa m’nthawi ya atumwi

Ningaonetse bwanji kuti nimalemekeza njila kapena kuti chanelo imene Yesu amaiseŵenzetsa popatsa anthu cakudya ca kuuzimu?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani