LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 June tsa. 7
  • Pewani Misampha Poceza ndi Anthu pa Intaneti

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Pewani Misampha Poceza ndi Anthu pa Intaneti
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Mabwenzi Anu a pa Intaneti ni Otani?
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Mkulu Wina wa za Umoyo Wacenjeza za Mavuto Amene Acinyamata Amakumana Nawo pa Soshomidiya—Kodi Baibo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
  • Kodi Masamba a Mcezo Akuwononga Mwana Wanu?—Mmene Baibo Ingathandizile Makolo
    Nkhani Zina
  • “Musamadziganizile Kuposa Mmene Muyenela Kudziganizila”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 June tsa. 7

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Pewani Misampha Poceza ndi Anthu pa Intaneti

Yesu akukana kusandutsa miyala kuti ikhale mikate

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Mofanana na zida zambili, mawebusaiti ocezelapo pa intaneti angakhale othandiza kapena owononga. Akhristu ena asankha kusaseŵenzetsa mawebusaiti ocezelapo. Ena amawaseŵenzetsa kuti aziceza na acibululu komanso anzawo. Komabe, Mdyerekezi amafuna kuti tiziseŵenzetsa mawebusaiti amenewa molakwika, zimene zingawononge mbili yathu na ubwenzi wathu na Yehova. Monga Yesu, tingaseŵenzetse mfundo za m’Mau a Mulungu kuti tidziŵe zimene zingativulaze na kuzipewa.—Luka 4:4, 8, 12.

MISAMPHA YOFUNIKA KUPEWA:

  • Kuseŵenzetsa intaneti mopitilila malile. Kuthela maola ambili tikuceza na anthu pa intaneti kungatiwonongele nthawi yofunika yocita zinthu zauzimu.

    Mfundo za m’Baibo: Aef. 5:15, 16; Afil. 1:10

  • Kutamba zinthu zokayikitsa. Kuyang’ana mapikica outsa cilako-lako kungacititse munthu kuyamba kutamba zamalice kapena kucita zaciŵelewele. Kuŵelenga nkhani zimene anthu ampatuko amafalitsa pa intaneti, kungawononge cikhulupililo cathu.

    Mfundo za m’Baibo: Mat. 5:28; Afil. 4:8

  • Kulemba mau osayenela kapena kuika mapikica osayenela. Cifukwa cakuti mtima ni wonyenga, munthu angayambe cizoloŵezi colemba mau osayenela kapena kuika mapikica osayenela pa intaneti. Kucita izi kungawononge mbili yake kapena kufooketsa cikhulupililo cake.

    Mfundo za m’Baibo: Aroma 14:13; Aef. 4:29

TAMBANI VIDIYO YAKUTI MUZISAMALA POCEZA NDI ANTHU PA INTANETI, NDIYENO KAMBILANANI MMENE MUNGAPEWELE ZOCITIKA ZOTSATILAZI:

Kawalala pa intaneti wadziŵa kuti eniake nyumba acokapo ali pacuti
Munthu wofuna kulemba nchito wina, waona mapikica osayenela amene munthuyo anaika pa intaneti
Waona mau oipa pa intaneti
Munthu wogona mocedwa cifukwa cokonda kuceza pa intaneti akulephela kuuka m’maŵa
    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani