LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 June tsa. 8
  • Moseŵenzetsela Makambilano Acitsanzo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Moseŵenzetsela Makambilano Acitsanzo
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Makambilano a Citsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Mmene Tingaseŵenzetsele Makambilano Acitsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Mmene Tingayambitsile Makambilano Pogwilitsila Nchito Mathirakiti
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Makambilano Acitsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 June tsa. 8

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Moseŵenzetsela Makambilano Acitsanzo

Kucokela mu January 2018, pacikuto ca Kabuku ka Misonkhano ya Umoyo na Utumiki Wathu pamakhala makambilano acitsanzo. Kodi makambilano amenewa tingaŵaseŵenzetse bwanji?

Mlongo apeleka nkhani ya m’sukulu pa misonkhano ya mkati mwa wiki.

Pokamba Nkhani ya M’sukulu: Muyenela kuseŵenzetsa funso, lemba, komanso ulalo, zimene zili pa makambilano acitsanzo. Komabe, zimenezi sizitanthauza kuti tifunika kucita kuloŵeza mawu a mu vidiyo ya makambilano acitsanzo. Mungaseŵenzetse mtundu wina wa makambilano, mawu oyamba, njila ina ya mafotokozedwe na zina zotelo. Mungagaŵilenso cofalitsa ca mu Thuboksi yathu, olo kuti sicinachulidwe mu malangizo a mbali imeneyo.

Mlongo mmodzi-modziyo ali mu ulaliki, aŵelenga lemba kwa mayi wina.

Pamene Tili Muulaliki: Makambilano acitsanzo anakonzedwa kuti azitipatsa malingalilo otithandiza. Ngati munthu waonetsa cidwi ceni-ceni ndipo afuna kudziŵa zambili, mungapitilize kukambilana naye mwina mwa kuseŵenzetsa makambilano acitsanzo a ulendo wobwelelako. Mungasintheko makambilano acitsanzo, kapena mungaseŵenzetse makambilano ena osiyana nawo. Kodi nkhani ya mwezi watha kapena lemba lina ingakope cidwi ca anthu a m’gawo lanu? Kodi anthu a kumene mukhala amacita cidwi kwambili na zocitika za posacedwa kapena kuti nyuzi? Mulimonse mmene mwasankhila kuseŵenzetsa makambilano acitsanzo, colinga canu cizikhala ‘kucita zinthu zonse cifukwa ca uthenga wabwino, kuti tiugawilenso kwa ena.’—1 Akor. 9:22, 23.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani