LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb22 July tsa. 16
  • Mmene Tingaseŵenzetsele Makambilano Acitsanzo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mmene Tingaseŵenzetsele Makambilano Acitsanzo
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Nkhani Zofanana
  • Moseŵenzetsela Makambilano Acitsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Makambilano a Citsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Mmene Tingayambitsile Makambilano Pogwilitsila Nchito Mathirakiti
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Konzani Ulaliki Wanu Wogaŵila Magazini
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
mwb22 July tsa. 16
Zithunzi: 1. Mlongo na mwamuna wake akuseŵenzetsa kabuku kakuti “Kondwelani na Moyo Kwamuyaya!” polalikila mayi panyumba pake. 2. Mlongo mmodzi-modziyo akucita citsanzo poseŵenzetsa kabuku kakuti “Kondwelani na Moyo Kwamuyaya!” pa msonkhano wa mkati mwa mlungu.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Mmene Tingaseŵenzetsele Makambilano Acitsanzo

Abale amagwila nchito yaikulu pokonza makambilano acitsanzo, ndipo ofalitsa ambili aona kuti makambilano amenewa ni othandiza kwambili m’magawo awo. Koma popeza mikhalidwe imasiyana-siyana padzikoli, pocita ulaliki ofalitsa ali na ufulu wosintha funso, lemba, na ulalo, ngakhalenso kugwilitsa nchito ulaliki wina umene ungakhale wocititsa cidwi kwa anthu a m’gawo lawo. Komabe, ngati kuli kampeni ya ulaliki, ofalitsa onse ayenela kutsatila malangizo amene apelekedwa. Colinga cathu ni kukwanilitsa nchito imene Yesu anatipatsa, yolalikila uthenga wabwino wa Ufumu.—Mat. 24:14.

Ofalitsa akamasamalila nkhani zawo za m’sukulu, makambilano awo atsamile (azikidwe) pa mfundo yaikulu ya makambilano acitsanzo a mu Kabuku ka Umoyo na Utumiki. (Mwacitsanzo, mu July na August, mfundo yaikulu ya makambilano acitsanzo ni kuonetsa colinga ca Mulungu kwa anthu.) Koma ofalitsa ni omasuka kugwilitsa nchito funso lina, lemba, ulalo, kapena mtundu wina wa makambilano amene angakhale othandiza m’gawo lanu, kupatulapo ngati papelekedwa malangizo akuti asasinthe zimenezi. Izi zasintha malangizo amene ali pa tsamba 8 m’kabuku ka misonkhano ka June 2020.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani